Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

JULY 19, 2019
UNITED STATES

Zokhudza Msonkhano Wamayiko wa 2019 Wakuti “Chikondi Sichitha,” ku Houston, United States (Chingelezi)

Zokhudza Msonkhano Wamayiko wa 2019 Wakuti “Chikondi Sichitha,” ku Houston, United States (Chingelezi)
  • Masiku: 12 mpaka 14 July, 2019

  • Malo: NRG Stadium ku Houston, Texas, United States

  • Zinenero: Chingelezi, Chikoleya

  • Chiwerengero cha Osonkhana: 50,901

  • Chiwerengero cha Obatizidwa: 401

  • Chiwerengero cha Alendo Ochokera ku Mayiko Ena: 5,000

  • Nthambi Zoitanidwa: Australasia, Belgium, Brazil, Britain, Canada, Colombia, Czech-Slovak, France, India, Italy, Japan, Korea, Philippines, ndi Scandinavia

  • Zina Zomwe Zinachitika: A Sylvester Turner, omwe ndi meya wa mzinda wa Houston, anachita chidwi kwambiri ndi a Mboni za Yehova 50,000 pamodzi ndi alendo awo omwe anabwera kumsonkhano wa ku Houston. Iwo anati: “Tinasangalala kwambiri kulandira a Mboni kuno ku Houston. Zinali ngati tatsegula mawindo kuti mpweya wabwino ulowe. Ngati [a Mboni za Yehova] mungamabwere kawiri pachaka, ndinu olandiridwa mumzinda uno wa Houston. Mudzabwerenso chaka chamawa, komanso chaka chinacho.”

 

Abale ndi alongo akulandira alendo ku Houston

Alendo akulalikira limodzi ndi abale ndi alongo a ku Houston

Ena mwa abale ndi alongo athu 401 atsopano akubatizidwa

M’bale Anthony Morris wa m’Bungwe Lolamulira akukamba nkhani yomaliza pa tsiku Loweruka

Alendo ochokera ku mayiko ena akujambulitsa, ndipo ena avala zovala zakwawo

Alendo akusangalala kukhala limodzi

Abale ndi alongo omwe ali muutumiki wanthawi zonse wapadera akusangalala pamene anthu akuwaombera m’manja pamapeto pa msonkhanowu pa tsiku Lamlungu

Abale ndi alongo a ku Houston ali papulatifomu pambuyo pa zochitika zosiyanasiyana zamadzulo monga kuimba, kuvina, komanso kufotokoza mwachidule zokhudza mbiri ya Mboni za Yehova ku Houston