Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

AUGUST 29, 2019
UNITED STATES

Zokhudza Msonkhano Wamayiko wa 2019 Wakuti “Chikondi Sichitha,” ku Houston, United States (Chisipanishi)

Zokhudza Msonkhano Wamayiko wa 2019 Wakuti “Chikondi Sichitha,” ku Houston, United States (Chisipanishi)
  • Masiku: 23 mpaka 25 August, 2019

  • Malo: NRG Stadium ku Houston, Texas, United States

  • Chinenero: Chisipanishi

  • Chiwerengero cha Osonkhana: 56,167

  • Chiwerengero cha Obatizidwa: 626

  • Chiwerengero cha Alendo Ochokera ku Mayiko Ena: 5,500

  • Nthambi Zoitanidwa: Argentina, Bolivia, Central America, Chile, Colombia, Dominican Republic, Ecuador, France, Italy, Japan, Peru, Philippines, Spain, Trinidad ndi Tobago, komanso Venezuela

  • Zina Zomwe Zinachitika: A Joelle Hardin omwe ndi mkulu woona zamalonda komanso kusungira malo makasitomala ku Space Center Houston anati: “M’mawawu mmodzi mwa anthu omwe ndimagwira nawo ntchito [yemwe ankachita sikani matikiti pamene alendo ankalowa] anabwera kwa ine n’kunena kuti: ‘Joelle, . . . aliyense amandiyang’ana n’kundiuza kuti, “Zikomo,” ndipo ena amandiuza zimenezi m’zinenero zina.’ Zimenezi zinachititsa kuti akhale wosangalala tsiku lonse. N’kale limene ndinamuona atasangalala kwambiri choncho.”

 

Alendo akufika pasitediyamu m’mawa

Alendo akulalikira limodzi ndi abale ndi alongo a ku Texas

Abale ndi alongo ambiri ongodzipereka akuyeretsa sitediyamu ya NRG Stadium Lachisanu msonkhano usanayambe

Awiri mwa abale ndi alongo 626 atsopano akubatizidwa

M’bale Mark Sanderson wa m’Bungwe Lolamulira akukamba nkhani yomaliza Lachisanu masana

Alendo akulemba notsi uku akumvetsera nkhani pa msonkhanowu

Mlongo akuonetsa alendo malo osungirako zinthu zakale a Houston Museum of Natural Science, pa ulendo wina wokaona malo womwe alendowa anapita

Abale ndi alongo athu akuvina pa zochitika zina zamadzulo

Abale ndi alongo omwe ali muutumiki wanthawi zonse wapadera ali m’bwalo la sitediyamu ndipo akubayibitsa pojambulitsa Lamlungu msonkhanowu utatha