Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

AUGUST 15, 2019
UNITED STATES

Zokhudza Msonkhano Wamayiko wa 2019 Wakuti “Chikondi Sichitha,” ku Phoenix, United States

Zokhudza Msonkhano Wamayiko wa 2019 Wakuti “Chikondi Sichitha,” ku Phoenix, United States
  • Masiku: 9 mpaka 11 August, 2019

  • Malo: Chase Field ku Phoenix, Arizona, United States

  • Chinenero: Chingelezi

  • Chiwerengero cha Osonkhana: 40,237

  • Chiwerengero cha Obatizidwa: 352

  • Chiwerengero cha Alendo Ochokera ku Mayiko Ena: 5,000

  • Nthambi Zoitanidwa: Australasia, Britain, Canada, Central Europe, Chile, France, Greece, India, Italy, Korea, Micronesia, Scandinavia, Sri Lanka, Tahiti, Thailand, Trinidad and Tobago, ndi Turkey

  • Zina Zomwe Zinachitika: A Steve Moore, omwe ndi pulezidenti ndiponso mkulu wa kampani ya Visit Phoenix yomwe imathandiza anthu kupeza malo ochitira misonkhano, mahotela komanso kokachitira holide m’dera la Phoenix, anati: “Ndakhala ndikugwira ntchitoyi kwa nthawi yayitali, ndipo [msonkhanowu] ndi umene wakonzedwa bwino kwambiri pa misonkhano yonse imene ndakhala ndi mwayi wogwira nawo ntchito. Kuonjezera pamenepo, mwalonjeza kuti muyeretsa sitediyamuyi musanapite, palibe amene amachita zimenezi.”

 

Alendo akulandiridwa ndi manja awiri pamene akufika pabwalo la ndege la Sky Harbor International Airport ku Phoenix

Abale ndi alongo a ku Phoenix akonzekera kuti alandire alendo ku imodzi mwa mahotela omwe alendowo anafikira

Abale ndi alongo mahandiredi ambiri akupereka moni mosangalala kwa alendo pamene akufika pa Chase Field Lachisanu m’mawa

Alendo akumvetsera msonkhano ndipo ena avala zovala za kwawo

Awiri mwa abale ndi alongo 352 atsopano akubatizidwa

M’bale Samuel Herd wa m’Bungwe Lolamulira akukamba nkhani yomaliza pa tsiku lachiwiri la msonkhanowu

Alendo akudzijambula pamene akuona malo ku nkhalango ya boma

Abale athu akwera ngolo yokokedwa ndi mahatchi ngati mbali yosonyeza mbiri ya tauni ina ya m’zaka za 1800 ku American West

Atumiki a nthawi zonse ochokera kumayiko ena ali m’bwalo la sitediyamu pamapeto pa msonkhano pa tsiku Lamlungu