Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

DECEMBER 9, 2015
UNITED STATES

A Mboni za Yehova Amaliza Kumanga Mbali Yaikulu ya Likulu Lawo Latsopano Lapadziko Lonse

A Mboni za Yehova Amaliza Kumanga Mbali Yaikulu ya Likulu Lawo Latsopano Lapadziko Lonse

NEW YORK—Kuyambira mwezi wa August mpaka October, 2015, ntchito yomanga likulu latsopano la Mboni za Yehova inafika pachimake. Pamalowa pankafika anthu ogwira ntchito ongodzipereka okwana 3,800 tsiku lililonse.

Nthawi yomwe ntchitoyi inafika pachimake, pamalowa pankafika mabasi 40 omwe ankanyamula anthu ogwira ntchito okwana 3,800 tsiku lililonse.

Malo 8 akhala akugwiritsidwa ntchito monga nyumba zodyeramo anthu ogwira ntchito pamalowa.

Kungoyambira mu July 2013, pomwe ntchito yomangayi inayamba, a Mboni oposa 18,000 akhala akufika kumalowa kudzagwira ntchito. A Mboniwa ankachokera m’madera osiyanasiyana a dziko la United States, monga ku Alaska ndiponso Hawaii. Anthu ambiri amabwera kudzagwira ntchito pamalowa kwa mlungu umodzi, iwiri, itatu kapena 4.

A Richard Devine, omwe ndi tcheyamani wa ntchito yomanga likulu latsopano ku Warwik, ananena kuti: “Pamalo ano pamabwera anthu ambirimbiri kudzagwira ntchito. Ndiye kuti zinthu ziziyenda bwino, tinakonza zoti anthu 400 azigwira ntchito kuyambira 3 koloko madzulo mpaka 2 koloko m’mawa.” Gawo lachiwiri la ntchitoyi linagwiridwa kuyambira mwezi wa May mpaka September.

Chithunzi chomwe chinajambulidwa dzuwa likulowa chosonyeza geti lolowera ku likulu latsopano la Mboni za Yehova.

Komiti yomwe ikuyang’anira ntchitoyi inanena kuti pa nyumba zogona 4 zomwe zikumangidwa, ziwiri zikhala zitamalizidwa pofika mu January 2016 monga mmene anakonzera. Komabe a Devine ananenanso kuti: “Ntchitoyi ikufulumira kwambiri kuposa mmene tinkaganizira, moti tayamba kugwira ntchito zimene tinkayenera kudzagwira miyezi 4 ikubwerayi. Izi zatheka chifukwa anthu ambiri akudzipereka kudzagwira ntchitoyi.” Panopa ntchito yomwe yatsala ndi kumanga nyumba imodzi yogona, nyumba imodzi yomwe mudzakhale maofesi komanso nyumba yokonzeramo zinthu. Tikuyembekezera kuti ntchito imeneyi idzakhala itatha pofika pa 1 September, 2016.

Chithunzi chojambulidwa m’mwamba chosonyeza likulu latsopano lapadziko lonse la Mboni za Yehova.

Yankhulani ndi:

Kuchokera ku Mayiko Ena: J. R. Brown, Office of Public Information, tel. +1 718 560 5000