YOBU 21-27
CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU |Yobu Anapewa Maganizo Olakwika
Satana amaseŵenzetsa mabodza pofuna kufooketsa atumiki a Yehova masiku ano. Onani mmene mabodza a Satana amasiyanilana ndi mmene Yehova amaonela zinthu, malinga ndi mmene buku la Yobu likuonetsela. Lembani mndandanda wa Malemba ena oonjezela amene angakuthandizeni kuona kuti Yehova amakusamalilani.
MABODZA A SATANA |
MMENE YEHOVA AMAONELA ZINTHU |
---|---|
Mulungu ndi wovuta kwambili kumusangalatsa, cakuti palibe ciliconse cimene atumiki ake amacita cimene iye amasangalala naco. Ngakhale cilengedwe sicimukondweletsa. (Yobu 4:18; 25:5) |
Yehova amayamikila kudzipeleka kwathu (Yobu 36:5) |
Munthu ndi wacabecabe kwa Mulungu (Yobu 22:2) |
Yehova amavomeleza ndi kudalitsa utumiki wathu umene timacita mokhulupilika (Yobu 33:26; 36:11) |
Mulungu alibe nazo nchito zakuti mukucita zinthu mwacilungamo (Yobu 22:3) |
Yehova amayang’anila anthu olungama ndi okhulupilika (Yobu 36:7) |