UMOYO WATHU WACIKRISTU
Zikumbutso za Msonkhano Wacigawo
Nthawi zonse timafuna kuonetsa kuti timakonda Mulungu ndi anzathu pa nthawi ya msonkhano wacigawo. (Mat. 22:37-39) Lemba la 1 Akorinto 13:4-8 limati: “Cikondi n’coleza mtima ndiponso n’cokoma mtima. Cikondi . . . sicicita zosayenela, sicisamala zofuna zake zokha, sicikwiya. . . . Cikondi sicitha.” Conco, pamene muonelela vidiyo ya Zikumbutso za Msonkhano Wacigawo, ganizilani njila zimene mungaonetsele cikondi kwa ena pa msonkhano wacigawo.
KODI TINGAONETSE BWANJI CIKONDI . . .
-
posungila ena malo okhala?
-
nyimbo za malimba zikayamba?
-
pamalo ogona m’dela limene mukucitikila msonkhano?
-
pogwila nchito yodzifunila?