Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU | YOBU 16-20

Limbikitsani Ena ndi Mau Abwino

Limbikitsani Ena ndi Mau Abwino

Zokamba zathu ziyenela kulimbikitsa ena

16:4, 5

  • Yobu anali wopsinjika maganizo ndi wothedwa nzelu, cakuti anafuna thandizo ndi cilimbikitso kwa ena

  • Anzake atatu a Yobu sanakambe mau alionse omulimbikitsa. M’malomwake, anamuimba mlandu ndi kuonjezela nkhawa zake

Mau oipa a Bilidadi anacititsa Yobu kulila mosautsidwa mtima

19:2, 25

  • Yobu analilila kwa Mulungu kuti amuthandize, ngakhale kum’pempha kuti afe

  • Yobu anali ndi ciyembekezo cakuti adzaukitsidwa, ndipo anapitiliza kupilila mokhulupilika