GENESIS 32-33
CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU |Kodi Mukulimbikila kuti Mupeze Madalitso?
32:24-28
Kuti tilandile dalitso la Yehova, tifunika kulimbikila kuika zinthu za Ufumu patsogolo mu umoyo wathu. (1 Akor. 9:26, 27) Pamene titumikila Yehova, tiyenela kukhala na mzimu umene Yakobo anaonetsa polimbana na mngelo. Tingaonetse kuti tifuna dalitso la Yehova mwa . . .
-
Kukonzekela bwino misonkhano ya mpingo
-
Kutengako mbali nthawi zonse mu ulaliki
-
Kuyesetsa kuthandiza ena mumpingo
Olo kuti zinthu n’zovuta mu umoyo wanu, osaleka kupemphela kwa Yehova kuti akuthandizeni. Komanso, limbikilani pom’tumikila ndipo adzakudalitsani.
Dzifunseni kuti: ‘Mu umoyo wanga, ni mbali ziti zimene nifunika kulimbikilapo kuti nilandile dalitso la Yehova?’