Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

December 31–January 6

MACHITIDWE 19-20

December 31–January 6
  • Nyimbo 103 na Pemphelo

  • Mawu Oyamba (3 min. olo kucepelapo)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

  • Mukhale Chelu ndi Kuyang’anila Gulu Lonse la Nkhosa”: (10 min.)

    • Mac. 20:28—Akulu amaŵeta mpingo wa Mulungu (w11 6/15 mape. 20-21 pala. 5)

    • Mac. 20:31—Pakakhala pofunikila, Akulu amapeleka cithandizo “usana ndi usiku” (w13 2/1 peji 31 pala. 15)

    • Mac. 20:35—Akulu afunika kukhala na mzimu wodzimana (bt peji 172 pala. 20)

  • Kufufuza Cuma ca Kuuzimu: (8 min.)

    • Mac. 19:9—Kodi Paulo anatipatsa citsanzo cotani pa nkhani yocita khama, ndiponso kusintha njila zolalikilila? (bt peji 161 pala. 11)

    • Mac. 19:19—Kodi Akhristu a ku Efeso anapeleka citsanzo cotani cimene tingatengele? (bt mape. 162-163 pala. 15)

    • Kodi imwe pacanu, kuŵelenga Baibo kwa wiki ino kwakuphunzitsani ciani za Yehova?

    • Ni cuma ca kuuzimu cina citi cimene mwapeza pa kuŵelenga Baibo kwa wiki ino?

  • Kuŵelenga Baibo: (4 min. olo kucepelapo) Mac. 19:1-20

CITANI KHAMA PA ULALIKI

  • Kubwelelako Kaciŵili: (3 min. olo kucepelapo) Yambani na makambilano acitsanzo. Gaŵilani mwininyumba kakhadi kongenela pa webusaiti ya JW.ORG.

  • Kubwelelako Kacitatu: (3 min. olo kucepelapo) Sankhani mwekha lemba na funso lokakambilana ulendo wotsatila.

  • Phunzilo la Baibo: (6 min. olo kucepelapo) jl phunzilo 15

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

  • Nyimbo 99

  • Phunzitsani Anyamata Amene Akukalamila Maudindo: (15 min.) Kukambilana. Tambitsani vidiyo imeneyi. Ndiyeno yankhani mafunso aya: Ni udindo wofunika kwambili uti umene akulu ali nawo mu mpingo? (Mac. 20:28) N’cifukwa ciani akulu afunika kupitiliza kuphunzitsa ena? Kodi akulu angatengele bwanji citsanzo ca mmene Yesu anali kuphunzitsila atumwi ake? Kodi abale amene a akuphunzitsidwa afunika kukhala na khalidwe lotani? (Mac. 20:35; 1 Tim. 3:1) Nanga kodi akulu angawaphunzitse zotani abale amenewa? Kodi akulu ayenela kuwaona bwanji abale amene iwo akuphunzitsa?

  • Phunzilo la Baibo la Mpingo: (30 min.) jy mutu 48

  • Kubwelelamo na Kuchulako za Wiki Yotsatila (3 min.)

  • Nyimbo 118 na Pemphelo