Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

February 12-18

MASALIMO 5-7

February 12-18

Nyimbo 118 na Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Khalanibe Okhulupilika Ngakhale Anthu Ena Azicita Zoipa

(Mph. 10)

Cifukwa ca zocita za ena, nthawi zina Davide sanali kukhala wacimwemwe (Sal. 6:​6, 7)

Iye anapempha Yehova kuti amuthandize (Sal. 6:​2, 9; w21.03 15 ¶7-8)

Cikhulupililo colimba cimene Davide anali naco pa Yehova, cinamuthandiza kukhalabe wokhulupilika (Sal. 6:10)

DZIFUNSENI KUTI, ‘Kodi cikhulupililo canga n’colimba moti ningakhalebe wokhulupilika ngakhale ena atamacita zoipa?’—w20.07 8-9 ¶3-4.

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Sal. 5:9—Kodi mmelo wa anthu oipa uli ngati manda otseguka m’lingalilo lotani? (it-1 995)

  • Pa kuŵelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zomwe mungakonde kutigaŵilako?

3. Kuŵelenga Baibo

(Mph. 4) Sal. 7:​1-11 (th phunzilo 10)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) NYUMBA NA NYUMBA. (lmd phunzilo 1 mfundo 3)

5. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 2) ULALIKI WAMWAYI. Popanda kumuchulila mfundo ya m’Baibo, pezani njila yacibadwa yoonetsela munthu kuti ndinu mmodzi wa Mboni za Yehova. (lmd phunzilo 2 mfundo 4)

6. Kubwelelako

(Mph. 2) NYUMBA NA NYUMBA. Mwininyumba akufuna kukangana nanu. (lmd phunzilo 4 mfundo 5)

7. Kufotokoza Zimene Mumakhulupilila

(Mph. 4) Citsanzo. ijwfq 64—Mutu: N’cifukwa Ciyani Mboni za Yehova Sizitengako Mbali pa Zikondwelelo Zonyadila Dziko Lawo? (lmd phunzilo 3 mfundo 4)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 99

8. Lipoti la Caka ca Utumiki

(Mph. 15) Kukambilana. Ŵelengani cilengezo cocokela ku ofesi ya nthambi cokhudza lipoti la caka ca utumiki. Kenaka, pemphani omvela kuti afotokoze zocitika zosangalatsa za mu Lipoti la Caka ca Utumiki ca 2023 la Mboni za Yehova Padziko Lonse. Funsani mafunso ofalitsa omwe munawakonzekeletsa, kuti asimbe zocitika zolimbikitsa za mu ulaliki m’caka capita ca utumiki.

9. Phunzilo la Baibo la Mpingo

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 83 na Pemphelo