LUKA 6-7
CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU |Tizipimila Ena Mowolowa Manja
6:38
Munthu wowolowa manja amapeleka mokondwela nthawi yake, mphamvu zake, na zinthu zake kuti athandize ena na kuwalimbikitsa.
-
Mau a Cigiriki amene anawamasulila kuti “khalani opatsa” atanthauza kucita cinthu mosalekeza
-
Ngati tikhala opatsa, ena adzatikhuthulila m’matumba athu “muyezo wabwino, wotsendeleka, wokhuchumuka ndi wosefukila.” Mau amenewa angatanthauze cizoloŵezi ca ogulitsa malonda amene amaikapo mbasela pa zinthu zimene munthu wagula