Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

Kodi Mumaona Kuti Nchito Yamanja si Yokuyenelelani?

Kodi Mumaona Kuti Nchito Yamanja si Yokuyenelelani?

Mkulu wa ansembe na abale ake sanadzione kuti anali apamwamba kwambili moti n’kulephela kumanga nawo mpanda wa Yerusalemu (Neh. 3:1)

Amuna ena otchuka sanadzicepetse kuti agwile nawo nchito yomanganso mpanda (Neh. 3:5; w06 2/1 10 ¶1)

Akazi oopa Mulungu anagwila nawo na mtima wonse nchito yolemetsa imeneyo (Neh. 3:12; w19.10 23 ¶11)

Nchito zambili zimene zimacitika mumpingo ni zamanja komanso zooneka ngati zapansi, ndipo nthawi zina ena sangaone nchitozo.—w04 8/1 18 ¶16.

DZIFUNSENI KUTI, ‘Kodi kugwila nchito zooneka ngati zapansi cifukwa ca uthenga wabwino nimakuona bwanji?’—1 Akor. 9:23.