July 22-28
MASALIMO 66-68
Nyimbo 7 na Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)
1. Yehova Amanyamula Katundu Wathu Tsiku na Tsiku
(Mph. 10)
Yehova amamvela mapemphelo athu na kuwayankha (Sal. 66:19; w23.05 12 ¶15)
Yehova amadziŵa zosoŵa za anthu ovutika (Sal. 68:5; w10-CN 12/1 23 ¶6; w09-CN 4/1 31 ¶1)
Iye amatithandiza tsiku lililonse (Sal. 68:19; w23.01 19 ¶17)
ZOFUNIKA KUZISINKHASINKHA: Kodi timamulola bwanji Yehova kunyamula katundu wathu?
2. Kufufuza Cuma Cauzimu
(Mph. 10)
-
Sal. 68:18—Mu Isiraeli wakale, kodi ndani anali “mphatso za amuna”? (w06-CN 6/1 10 ¶5)
-
Pa kuŵelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?
3. Kuŵelenga Baibo
(Mph. 4) Sal. 66:1-20 (th phunzilo 11)
4. Kuyambitsa Makambilano
(Mph. 3) KUNYUMBA NA NYUMBA. Mwini nyumba ni wacikhalidwe cosiyana na canu. (lmd phunzilo 5 mfundo 3)
5. Kubwelelako
(Mph. 4) KUNYUMBA NA NYUMBA. Pitilizani kukambilana kathilakiti kamene munamusiyila ulendo wapita. (lmd phunzilo 9 mfundo 3)
6. Kupanga Ophunzila
Nyimbo 102
7. Kodi Mungam’peputsileko Katundu Mkhristu Mnzanu?
(Mph. 15) Kukambilana.
Palibe mtumiki wa Mulungu yemwe amakhala yekha akamalimbana na mavuto. (2 Mbiri 20:15; Sal. 127:1) Yehova ni Mthandizi wathu. (Yes. 41:10) Kodi Yehova amatithandiza m’njila ziti? Amatipatsa malangizo poseŵenzetsa mawu ake na gulu lake. (Yes. 48:17) Amatipatsanso mzimu wake woyela wamphamvu. (Luka 11:13) Amagwilitsa nchito abale na alongo athu kuti atilimbikitse na kutithandiza. (2 Akor. 7:6) Izi zionetsa kuti Yehova angagwilitse nchito aliyense wa ife kupeputsako katundu wa Mkhristu mnzake.
Tambitsani VIDIYO yakuti Onetsani Cikondi Cosatha mu Mpingo—Kwa Okalamba. Kenako funsani omvela kuti:
-
Kodi mungacite ciyani kuti mum’peputsileko katundu Mkhristu wokalamba?
Tambitsani VIDIYO yakuti Onetsani Cikondi Cosatha mu Mpingo—Kwa Atumiki Anthawi Zonse. Kenako funsani omvela kuti:
-
Kodi mungacite ciyani kuti mum’peputsileko katundu mtumiki wanthawi zonse?
Tambitsani VIDIYO yakuti Onetsani Cikondi Cosatha mu Mpingo—Kwa Alendo Ocokela ku Maiko Ena. Kenako funsani omvela kuti:
-
Kodi mungacite ciyani kuti muŵapeputsileko katundu anthu amene akukumana na mayeso ovuta?
8. Phunzilo la Baibo la Mpingo
(Mph. 30) bt mutu 13 ¶1-7, mawu oyamba a cigawo 5, komanso bokosi pa tsa. 103