AGALATIYA 4-6
CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU |Nkhani ‘Yophiphilitsila’ Yokhala na Tanthauzo kwa Ife
4:24-31
Mtumwi Paulo anasimba nkhani ‘yophiphilitsila,’ pofuna kuonetsa kuti pangano latsopano n’labwino kuposa pangano la Cilamulo. Khristu pamodzi na olamulila anzake adzatiyang’anila mwacikondi. Ndipo tonse tidzamasulidwa ku ucimo, kupanda ungwilo, mavuto, komanso imfa.—Yes. 25:8, 9.
HAGARA—KAPOLO WAMKAZI Isiraeli wakuthupi amene anali m’pangano la Cilamulo. Likulu lake linali Yerusalemu |
SARA—MFULU Yerusalemu wakumiyamba, amene ni gawo lakumwamba la gulu la Mulungu |
“ANA” A HAGARA Ayuda (amene analonjeza kuti azitsatila pangano la Cilamulo) anazunza Yesu, ndipo anamukana |
“ANA” A SARA Khristu na Akhristu odzozedwa okwana 144,000 |
UKAPOLO KU PANGANO LA CILAMULO Cilamuloci cinali kukumbutsa Aisiraeli kuti anali akapolo a ucimo |
PANGANO LATSOPANO LIMATIPATSA UFULU Kukhulupilila nsembe ya Khristu kunabweletsa ufulu wotimasula ku ukapolo wa Cilamulo |