YOBU 11-15
CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU |Yobu Anali ndi Cikhulupililo Cakuti Akufa Adzauka
Yobu anaonetsa kuti anali ndi cikhulupililo cakuti Mulungu adzamuukitsa
14:7-9, 13-15
-
Yobu anaonetsa cikhulupililo cake cakuti Mulungu adzaukitsa akufa pamene anayelekezela ciyembekezoco ndi mtengo, mwina wa maolivi
-
Mtengo wa maolivi akaudula umaphukanso cifukwa cakuti mizu yake imapita pansi kwambili ndiponso imayala malo aakulu. Ngati mizu yake ikali bwino, mtengowu sulephela kuphuka
-
Mvula ikagwa pambuyo pa cilala coopsa, mizu ya citsa couma ca mtengo wa maolivi imaphuka n’kukhala ndi “nthambi ngati mtengo watsopano”