Aitanila anthu ku Cikumbutso ku Slovenia

UMOYO NA UTUMIKI WATHU–KABUKU KA MISONKHANO March 2018

Makambilano Acitsanzo

Makambilano ozikidwa pa kampeni yoitanila anthu ku Cikumbutso na mafunso akuti: N’cifukwa ciani Yesu anafa? Kodi dipo limatheketsa ciani?

CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU

“Aliyense Wofuna Kukhala Wamkulu Pakati Panu Ayenela Kukhala Mtumiki Wanu”

Pamene ticita mautumiki osiyana-siyana, kodi colinga cathu n’cakuti tichuke na kutamandidwa? Nthawi zambili mtumiki wodzicepetsa amacita nchito zimene sizionekela kwa anthu ena koma kwa Yehova Mulungu cabe.

CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU

Muzitsatila Malamulo Aŵili Aakulu a m’Cilamulo

Kodi Yesu anakamba kuti malamulo aŵili aakulu a m’Cilamulo opezeka m’Baibo ni ati? Tingaonetse bwanji kuti timamvela malamulo amenewa?

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Tingacite Ciani Kuti Tikulitse Cikondi Cathu kwa Mulungu na kwa Mnansi Wathu

Tifunika kukonda Mulungu na mnansi wathu. Njila imodzi imene ingatithandize kukulitsa khalidwe la cikondi ni mwa kuŵelenga Baibo tsiku na tsiku.

CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU

Khalanibe Ogalamuka m’Masiku Otsiliza Ano

Masiku ano, kufuna-funa zinthu za kuthupi kwacititsa anthu ambili kulephela kucita zinthu zauzimu. Kodi Akhristu ogalamuka mwauzimu amasiyana bwanji ndi anthu a ku dziko?

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Tili ku Mapeto a Dongosolo Lino la Zinthu

Kodi mau a Yesu aonetsa bwanji kuti tikukhala m’nthawi ya mapeto? Funso ili pamodzi na ena ayankhiwa m’vidiyo yakuti Tili ku Mapeto a Dongosolo Lino la Zinthu.

CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU

“Khalanibe Maso”

M’fanizo la anamwali 10, kodi mkwati, anamwali ocenjela, ndi anamwali opusa aimila ndani? Nanga kodi fanizo limeneli likukhudzani bwanji?

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Kunola Luso Lathu mu Ulaliki​—Kuthandiza Maphunzilo Athu a Baibo Kukonzekela

Tikangokhazikitsa phunzilo, tiziwathandiza ophunzila athu kukhala na cizoloŵezi cokonzekela phunzilo. Tingacite bwanji zimenezi?