March 26–April 1
MATEYU 25
Nyimbo 143 na Pemphelo
Mau Oyamba (3 min. olo kucepelapo)
CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU
“Khalanibe Maso”: (10 min.)
Mat. 25:1-6—Anamwali asanu anzelu ndi anamwali asanu opusa anapita kukacingamila mkwatibwi
Mat. 25:7-10—Anamwali opusa sanalipo pamene mkwatibwi anafika
Mat. 25:11, 12—Anamwali ocenjela okha ndi amene analolewa kungena m’nyumba imene munali phwando la cikwati
Kufufuza Cuma ca Kuuzimu: (8 min.)
Mat. 25:31-33—Fotokozani fanizo la nkhosa na mbuzi (w15 3/15 peji 27 pala. 7)
Mat. 25:40—Tingaonetse bwanji kuti ndise mabwenzi a abale a Khristu? (w09 10/15 peji. 16 mapa. 16-18)
Kodi imwe pacanu, kuŵelenga Baibo kwa wiki ino kwakuphunzitsani ciani za Yehova?
Ni cuma ca kuuzimu cina citi cimene mwapeza pa kuŵelenga Baibo kwa wiki ino?
Kuŵelenga Baibo: (4 min. olo kucepelapo) Mat. 25:1-23
CITANI KHAMA PA ULALIKI
Kubwelelako Kaciŵili: (3 min. olo kucepelapo) Yambani na makambilano acitsanzo. Itanilani munthuyo ku Cikumbutso.
Kubwelelako Kacitatu: (3 min. olo kucepelapo) Sankhani mwekha lemba na kugaŵila cofalitsa cophunzitsila Baibo.
Nkhani: (6 min. olo kucepelapo) w15 3/15 peji 27 mapa. 7-10—Mutu: Kodi Fanizo la Nkhosa na Mbuzi Limagogomezela Bwanji Nchito Yolalikila?
UMOYO WATHU WACIKHRISTU
“Kunola Luso Lathu mu Ulaliki—Kuthandiza Maphunzilo Athu a Baibo Kukonzekela”: (10 min.) Kukambilana. Pambuyo pake, tambitsani na kukambilana vidiyo yoonetsa wofalitsa akuthandiza wophunzila Baibo mmene angakonzekelele phunzilo. Pemphani omvela kuti afotokoze njila zina zimene aseŵenzetsapo pothandiza ophunzila Baibo kukonzekela phunzilo.
Kulandila Alendo Athu: (5 min.) Nkhani yozikidwa mu Kabuku ka Umoyo na Utumiki ka March 2016. Fotokozani zocitika zokondweletsa zimene zinacitika pa nyengo ya Cikumbutso mu 2017. Kumbutsani onse za koika mamotoka, koloŵela mu holo na kotulukila, na mbali zina zofunika pa Cikumbutso cimene cidzacitika pa March 31.
Phunzilo la Baibo la Mpingo: (30 min.) jy mutu 14
Kubwelelamo na Kuchulako za Wiki Yotsatila (3 min.)
Nyimbo 79 na Pemphelo