CITANI KHAMA PA ULALIKI | WONJEZELANI CIMWEMWE CANU MU ULALIKI
Seŵenzetsani Mawu a Mulungu
Mawu a Mulungu ni amphamvu! (Aheb. 4:12) Angafike pamtima ngakhale anthu amene sadziŵa Mulungu. (1 Ates. 1:9; 2:13) Timapeza cimwemwe cacikulu ngati winawake wakondwela na mfundo inayake ya coonadi ca m’Baibo imene tamuonetsa.
ONELELANI VIDIYO YAKUTI PEZANI CIMWEMWE PA NCHITO YOPANGA OPHUNZILA—NOLANI MALUSO ANU—LOLANI MPHAMVU YA MAWU A MULUNGU KUGWILA NCHITO, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AWA:
-
Kodi mlongo Neeta walola bwanji mphamvu ya Mawu a Mulungu kugwila nchito pothandiza Rose kuona kufunika kofufuza m’Mawu a Mulungu?
-
Kodi Neeta walola bwanji mphamvu ya Mawu a Mulungu kugwila nchito mwa kuŵelenga lemba mokweza na kufotokoza cabe mfundo yofunika pa lembalo?
-
N’ciani cimene cionetsa kuti lemba lamufika pamtima Rose? Nanga muona kuti zimenezi zamukhudza bwanji Neeta?