UMOYO WATHU WACIKHRISTU
Muzipanga Zosankha Mwanzelu pa Nkhani ya Moŵa
Akhristu onse ayenela kudziletsa pankhani ya kumwa zakumwa zoledzeletsa. (Miy. 23:20, 29-35; 1 Akor. 6:9, 10) Ngati Mkhristu wasankha kumwako moŵa, ayenela kucita zimenezo mwacikatikati. Ayenelanso kupewa kudalila moŵa pocita zinthu. Komanso, ayenela kupewa kukhumudwitsa ena. (1 Akor. 10:23, 24; 1 Tim. 5:23) Conco, tiyenela kupewa kukakamiza aliyense kumwa moŵa, maka-maka acinyamata.
ONETSANI VIDIYO YA ZITHUNZI ZOJAMBULA PAMANJA YAKUTI GANIZILANI ZOTULUKAPO ZA KUMWA MOŴA, KENAKO YANKHANI MAFUNSO AWA:
-
N’cifukwa ciani Akhristu onse ayenela kutsatila malamulo a boma okhudza kumwa moŵa?—Aroma 13:1-4
-
N’cifukwa ciani sitiyenela kulola ena kutikakamiza kumwa moŵa?—Aroma 6:16
-
Pankhani ya moŵa, kodi mungapewe bwanji zocitika zimene zingakugwetseleni m’mavuto?