CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU
Musalole Zilakolako Zoipa Kukulamulilani
Davide analola cilakolako coipa kukula mu mtima mwake (2 Sam. 11:2-4; w21.06 17 ¶10)
Davide anaseŵenzetsa mphamvu zake molakwika pofuna kubisa chimo lake (2 Sam. 11:5, 14, 15; w19.09 17 ¶15)
Davide anakumana na mavuto aakulu cifukwa ca chimo lake (2 Sam. 12:9-12; w18.06 17 ¶7)
Kuti tipewe kuyang’ana kapena kuganizila zinthu zoipa, tifunika kudziletsa. (Agal. 5:16, 22, 23) Yehova angatithandize kuti tisamalole zilakolako zoipa kuzika mizu mu mtima mwathu.
DZIFUNSENI KUTI, ‘Kodi niyenela kulamulila maganizo anga makamaka pa mbali ziti?’