UMOYO WATHU WACIKHRISTU
“Cikondi . . . Cimayembekezela Zinthu Zonse”
Cifukwa tili na cikondi copanda dyela, timawafunila zabwino abale athu. (1 Akor. 13:4, 7) Mwacitsanzo, ngati m’bale wacita chimo ndipo wapatsidwa cilango, timakhala na ciyembekezo cakuti adzacitapo kanthu na kusintha. Timaleza nawo mtima aja ofooka m’cikhulupililo, ndipo timayesetsa kuwathandiza. (Aroma 15:1) Ngati wina wasankha kucoka mumpingo, sitileka kuyembekezela kuti tsiku lina adzabwelela.—Luka 15:17, 18.
ONELELANI VIDIYO YAKUTI KUMBUKILANI MMENE CIKONDI CILILI—CIMAYEMBEKEZELA ZINTHU ZONSE, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:
-
Kodi Abineri anasintha n’kukhala wokhulupilika kwa ndani? Fotokozani
-
Kodi Davide analilandila bwanji pempho la Abineri? Nanga Yowabu analilandila motani?
-
N’cifukwa ciyani tiyenela kuwafunila zabwino abale athu?