UMOYO WATHU WACIKHRISTU
Yehova Adziŵa zimene Tifunikila
Kapolo wokhulupilika ndi wanzelu amatipatsa cakudya “pa nthawi yoyenela,” kuonetsa kuti Yehova, amene akutsogolela kapoloyo, adziŵa zimene timafunikila mwauzimu. (Mat. 24:45) Cakudya ca pa nthawi yoyenela ciphatikizapo misonkhano yacigawo na misonkhano ya mkati mwa wiki.
TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI LIPOTI YA 2017 YA KOMITI YOYANG’ANILA NCHITO YOPHUNZITSA, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:
-
N’ndani amene ayenela kulandila citamando kaamba ka misonkhano yacigawo ya pa nthawi yake imene timakhala nayo? Cifukwa ciani?
-
Kodi nchito yokonzekela msonkhano wacigawo imayamba liti?
-
Kodi amasankha bwanji mitu na nkhani za misonkhano yacigawo?
-
Kodi pamakhala nchito zotani pokonzekela misonkhano yacigawo?
-
Kodi njila zophunzilila za m’sukulu ya Giliyadi amaziseŵenzetsa bwanji pokonza nkhani zophunzila pa misonkhano ya mkati mwa wiki?
-
Kodi madipatimenti osiyana-siyana amaseŵenzela bwanji pamodzi pokonza kabuku ka misonkhano?
Kodi mumamvela bwanji cifukwa ca zinthu zauzimu zimene Yehova amatipatsa?