UMOYO WATHU WACIKHRISTU
Akhristu Oona Amadziŵika na Cikondi—Pewani Kunyada na Mkwiyo
CIFUKWA CAKE N’KOFUNIKA: Yesu anaphunzitsa kuti ophunzila ake adzadziŵika cifukwa ca cikondi. (Yoh. 13:34, 35) Kuti tionetse cikondi monga ca Khristu, tifunika kuika zofuna za ena patsogolo na kupewa kukwiya. —1 Akor. 13:5.
MMENE TINGACITILE:
-
Ngati munthu wina wakamba kapena kucita zokukwiyitsani, yambani mwaima na kuganizila zimene zam’pangitsa kuti akambe kapena kucita zimenezo. Ganizilaninso zotulukapo za zimene mufuna kucita.—Miy. 19:11
-
Kumbukilani kuti tonse ndise opanda ungwilo, ndipo nthawi zina tingakambe kapena kucita zinthu zimene pambuyo pake tingadziimbe nazo mlandu
-
Mukasemphana maganizo, muzithetsa nkhani mwamsanga
TAMBANI VIDIYO YAKUTI “MUZIKONDANA”—PEWANI KUNYADA NDI KUCITA ZOSAYENELA, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:
-
Kodi m’bale Larry anaonetsa bwanji kuti sanakondwele na lingalilo la m’bale Tom?
-
Kodi kuyamba waima kuti aganizilepo kunam’thandiza bwanji mbale Tom kuti apewe kukwiya?
-
Kodi kuyankha modekha kwa m’bale Tom kunathandiza bwanji?