UMOYO WATHU WACIKHRISTU
Akhristu Oona Amadziŵika na Cikondi—Kuteteza Mgwilizano Wathu Wapadela
CIFUKWA CAKE N’KOFUNIKA: Usiku wakuti maŵa Yesu aphedwa, anapemphela kuti ophunzila ake “akhale mu umodzi weni-weni.” (Yoh. 17:23) Kuti tikhale ogwilizana, tifunika kuonetsana cikondi cimene “sicisunga zifukwa.”—1 Akor. 13:5.
MMENE TINGACITILE:
-
Tengelani citsanzo ca Yehova mwa kuyang’ana zabwino mwa ena
-
Muzikhululukila ena na mtima wonse
-
Mukakambilana ndipo nkhaniyo yatha, osaiutsanso.—Miy. 17:9
TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI “MUZIKONDANA”—MUSAMASUNGE ZIFUKWA, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:
-
M’mbali yoyamba ya vidiyo, kodi Helen anaonetsa bwanji kuti anali ‘kusunga zifukwa’?
-
M’mbali yaciŵili ya vidiyo, kodi Helen anacita ciani kuti agonjetse maganizo oipa na kukhala na maganizo oyenela?
-
Kodi Helen anathandizila bwanji kuti mpingo ukhale wogwilizana?