Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU | SALIMO 119

“Muzitsatila Cilamulo ca Yehova”

“Muzitsatila Cilamulo ca Yehova”

Kutsatila cilamulo ca Yehova kutanthauza kumvela malangizo a Mulungu ndi mtima wonse. M’Baibulo muli zitsanzo zambili za anthu amene anali kutsatila ndi kudalila cilamulo ca Yehova monga mmene wamasalimo anacitila.

Kutsatila cilamulo ca Mulungu n’kumene kumatipatsa cimwemwe ceni-ceni

119:1-8

Yoswa anali kudalila kwambili malangizo a Yehova. Anadziŵa kuti ngati afuna kukhala wacimwemwe ndi kuti zinthu zimuyendele bwino, anafunika kukhulupilila Yehova na mtima wake wonse

Mawu a Mulungu amatithandiza kuti tikhale olimba mtima polimbana ndi ziyeso

119:33-40

Yeremiya anaonetsa kuti anali wolimba mtima ndipo anadalila Yehova ngakhale kuti anakumana ndi mavuto. Anapitiliza kukhala na umoyo wosalila zambili ndi kugwila nchito imene anapatsidwa.

Kudziŵa bwino Mawu a Mulungu kumatithandiza kulalikila molimba mtima

119:41-48

Paulo sanacite mantha kuuza aliyense uthenga wocokela kwa Mulungu. Iye anali kukhulupilila kuti Yehova adzamuthandiza kulalikila molimba mtima kwa Bwanamkubwa Felike

Ni pa zocitika ziti pamene ningaonetse kulimba mtima polaliki ena?

  • Kusukulu

  • Kunchito

  • Kwa Acibale

  • Kwina