Onetsani Cikondi Canu kwa Mulungu
Phunzilo 16
Onetsani Cikondi Canu kwa Mulungu
Kuti ubwenzi wanu na munthu wina upitilize, mufunikila kumakambitsana. Mumamumvela, nayenso amakumvelani. Ndiponso, mumauzako anthu ena zinthu zabwino ponena za iye. Ni cimodzimodzi na kukhala mnzake wa Mulungu. Onani zimene Baibo imakamba pankhani imeneyi:
Muzikamba na Yehova m’pemphelo nthawi zonse. “Limbikani cilimbikile m’kupemphela.”—Aroma 12:12.
Muziŵelenga Mau a Mulungu, Baibo. “Lemba lililonse adaliuzila Mulungu, ndipo lipindulitsa pa ciphunzitso, citsutsano, cikonzelo, cilangizo ca m’cilungamo.”—2 Timoteo 3:16.
Muziphunzitsa ena za Mulungu. “Cifukwa cake mukani, phunzitsani anthu a mitundu yonse, . . . asunge zinthu zonse zimene ndinakulamulilani inu.”—Mateyu 28:19, 20.
Miyambo 13:20.
Khalani mnzawo wa aja amene ni anzake a Mulungu. “Ukayenda ndi anzelu udzakhala wanzelu.”—Muzipezeka kumisonkhano ku Nyumba ya Ufumu. ‘Tiyeni tiganizilane wina ndi mnzake, kuti tilimbikitsane pa cikondi ndi nchito zabwino.’—Ahebri 10:24, NW.
Muzithandiza panchito ya Ufumu na zopeleka zanu. ‘Yense acite monga atsimikiza mtima, si mwa cisoni kapena mokakamiza, pakuti Mulungu akonda opeleka mokondwelela.’—2 Akorinto 9:7.