PHUNZILO 1
Mawu Oyamba Ogwila Mtima
Machitidwe 17:22
ZOFUNIKILA: Mawu anu oyamba afunika kukopa cidwi, kuchula nkhani yanu, komanso kuonetsa mmene nkhaniyo ikuwakhudzila omvela anu.
MOCITILA:
-
Kukopa cidwi. Sankhani funso, mfundo, cocitika, kapena nkhani ya pa nyuzi imene omvela anu angacite nayo cidwi.
-
Chulani nkhani yanu. Onetsetsani kuti mawu anu oyamba akumveketsa bwino nkhani yanu kwa omvela, na colinga ca ulaliki wanu.
-
Onetsani cifukwa cake nkhaniyo ni yofunika. Kambani zinthu zothandizadi kwa omvela anu. Afunika kumvetsa bwino-bwino mmene nkhaniyo ingawathandizile.