PHUNZILO 16
Khalani Wolimbikitsa Komanso Wotsitsimula
Yobu 16:5
ZOFUNIKILA: Muzikamba zinthu zothandiza komanso zolimbikitsa.
MOCITILA:
-
Khalani na cidalilo mwa omvela anu. Dalilani kuti iwo ali na mtima wofuna kukondweletsa Yehova. Ngakhale pofuna kupeleka uphungu, coyamba pezani cowayamikila moona mtima.
-
Cepetsani kukamba pa zinthu zoipa. Chulani zoipa m’nkhani yanu mongofuna kumveketsa mfundo inayake. Koma mzimu wonse wa nkhani yanu uzikhala pa zinthu zabwino.
-
Seŵenzetsani kwambili Mawu a Mulungu. Unikani zimene Yehova anacita, zimene akucita, na zimene adzacitila anthu. Apatseni ciyembekezo omvela anu na kuwalimbikitsa.