PHUNZILO 9
Kuseŵenzetsa Bwino Zitsanzo Zooneka
Genesis 15:5
ZOFUNIKILA: Kuti mumveketse bwino mfundo zofunika mungaseŵenzetse zitsanzo za zinthu zooneka.
MOCITILA:
-
Sankhani zinthu zooneka zothandizila kuphunzitsa. Mungaseŵenzetse mapikica, zithunzi, mapu, chati ya nthawi, na zinthu zina zooneka, kotelo kuti mumveketse mfundo zofunika, osati tumfundo tung’ono-tung’ono. Onetsetsani kuti omvela anu asakumbukile citsanzo cooneka cokhaco, koma maka-maka phunzilo lake.
-
Tsimikizani kuti omvela anu akutha kuciona bwino citsanzo coonekaco.