Mawu Oyamba a Cigawo 10
Yehova ni Mfumu ya cilengedwe conse. Iye nthawi zonse wakhala akulamulila, ndipo adzalamulilabe kwamuyaya. Mwacitsanzo, anapulumutsa Yeremiya m’citsime cozama. Anapulumutsa Sadirake, Mesake na Abedinego m’ng’anjo ya moto, komanso Danieli m’dzenje la mikango. Yehova anateteza Esitere kuti apulumutse anthu onse a mtundu wake. Iye sadzalola kuti zoipa zipitilize kwamuyaya. Maulosi okhudza fano lalikulu komanso mtengo waukulu, amatitsimikizila kuti Ufumu wa Yehova posacedwa udzacotsapo zoipa zonse na kuyamba kulamulila pa dziko lapansi.
M'CIGAWO CINO
PHUNZILO 57
Yehova Atumiza Yeremiya Kuti Akalalikile
Zimene mneneli wacicepele uyu anakamba, zinawakwiitsa kwambili akulu-akulu a Yuda.
PHUNZILO 58
Yerusalemu Awonongedwa
Ayuda apitiliza kulambila milungu yabodza, ndiyeno Yehova awasiya.
PHUNZILO 59
Anyamata Anayi Amene Anamvela Yehova
Anyamata aciyuda sanaleke kukhulupilila Yehova, ngakhale ali ku nyumba kwa mfumu nebukadinezara ku Babulo.
PHUNZILO 60
Ufumu Umene Udzalamulila Kwamuyaya
Danieli amasulila tanthauzo la maloto odabwitsa a Nebukadinezara.
PHUNZILO 61
Anakana Kugwadila Fano
Sadirake, Mesake, na Abedinego akana kulambila fano lagolide la mfumu ya Babulo.
PHUNZIIO 62
Ufumu Umene Uli Monga Mtengo Waukulu
Maloto a Nebukadinezara alosela za tsogolo la iye mwini.
PHUNZILO 63
Dzanja Lilemba pa Cipupa
Kodi mawu osadziŵika anaonekela pa nthawi iti? Nanga atanthauza ciani?
PHUNZILO 64
Danieli Aponyedwa m’Dzenje la Mikango
Pemphelani kwa Yehova tsiku lililonse, monga mmene Danieli anali kucitila!
PHUNZILO 65
Mfumukazi Esitere Apulumutsa Anthu a Mtundu Wake
Ngakhale kuti anali ku dziko la eni, zinthu zinasintha kucoka pa mwana wamasiye n’kukhala mfumukazi.
PHUNZILO 66
Ezara Aphunzitsa Cilamulo ca Mulungu
Aisiraeli atamvetsela kwa Ezara, iwo anapanga lonjezo lapadela kwa Mulungu.
PHUNZILO 67
Mpanda wa Yerusalemu Umangidwanso
Nehemiya anadziŵa kuti adani ake afuna kuukila. Koma n’cifukwa ciani sanacite mantha?