Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Mawu Oyamba a Cigawo 13

Mawu Oyamba a Cigawo 13

Yesu anabwela pa dziko lapansi kudzapeleka moyo wake kaamba ka anthu opanda ungwilo. Ngakhale anafa, iye anagonjetsa dziko. Yehova anakhulupilika kwa Mwana wake, ndipo anamuukitsa atamwalila. Mpaka imfa yake, Yesu modzicepetsa anali kutumikila ena, ndipo anali kuwakhululukila akalakwitsa. Yesu ataukitsidwa, anaonekelanso kwa ophunzila ake. Anawaphunzitsa mmene angagwilile nchito yofunika kwambili imene anawapatsa. Ngati ndimwe kholo, thandizani mwana wanu kudziŵa kuti, ngakhale masiku ano, tili na mwayi wotengako mbali m’nchito imeneyo.

M'CIGAWO CINO

PHUNZILO 87

Mgonelo wa Ambuye

Yesu apeleka malangizo ofunika kwa atumwi ake.

PHUNZILO 88

Am’gwila Yesu

Yudasi Isikariyoti atsogolela cigulu ca anthu cokhala na malupanga na zibonga kuti akagwile Yesu.

PHUNZILO 89

Petulo Akana Yesu

Kodi n’ciani cicitika m’bwalo la nyumba ya Kayafa? Nanga n’ciani cicitikila Yesu m’nyumba ya Kayafa?

PHUNZILO 90

Yesu Aphedwa ku Gologota

N’cifukwa ciani Pilato walamula kuti Yesu aphedwe?

PHUNZILO 91

Yesu Aukitsidwa

Kodi ni zinthu zodabwitsa ziti zimene zicitika pambuyo pakuti Yesu waphedwa?

PHUNZILO 92

Yesu Aonekela kwa Ophunzila Ake Asodzi

Kodi Yesu acita ciani kuti ophunzila ake amumvetsele?

PHUNZILO 93

Yesu Abwelela Kumwamba

Asanabwelele, apatsa ophunzila ake malangizo ena ofunika kwambili.