Mawu Oyamba a Cigawo 13
Yesu anabwela pa dziko lapansi kudzapeleka moyo wake kaamba ka anthu opanda ungwilo. Ngakhale anafa, iye anagonjetsa dziko. Yehova anakhulupilika kwa Mwana wake, ndipo anamuukitsa atamwalila. Mpaka imfa yake, Yesu modzicepetsa anali kutumikila ena, ndipo anali kuwakhululukila akalakwitsa. Yesu ataukitsidwa, anaonekelanso kwa ophunzila ake. Anawaphunzitsa mmene angagwilile nchito yofunika kwambili imene anawapatsa. Ngati ndimwe kholo, thandizani mwana wanu kudziŵa kuti, ngakhale masiku ano, tili na mwayi wotengako mbali m’nchito imeneyo.
M'CIGAWO CINO
PHUNZILO 88
Am’gwila Yesu
Yudasi Isikariyoti atsogolela cigulu ca anthu cokhala na malupanga na zibonga kuti akagwile Yesu.
PHUNZILO 89
Petulo Akana Yesu
Kodi n’ciani cicitika m’bwalo la nyumba ya Kayafa? Nanga n’ciani cicitikila Yesu m’nyumba ya Kayafa?
PHUNZILO 91
Yesu Aukitsidwa
Kodi ni zinthu zodabwitsa ziti zimene zicitika pambuyo pakuti Yesu waphedwa?
PHUNZILO 92
Yesu Aonekela kwa Ophunzila Ake Asodzi
Kodi Yesu acita ciani kuti ophunzila ake amumvetsele?
PHUNZILO 93
Yesu Abwelela Kumwamba
Asanabwelele, apatsa ophunzila ake malangizo ena ofunika kwambili.