Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Mawu Oyamba a Cigawo 8

Mawu Oyamba a Cigawo 8

Yehova anadalitsa Solomo mwa kum’patsa nzelu zoculuka, na mwayi womanga kacisi. Koma m’kupita kwa nthawi, iye anasiya Yehova. Ngati ndimwe kholo, m’fotokozeleni mwana wanu zimene zinapangitsa Solomo kuti asiye Mulungu. Ufumu unagaŵika, ndipo mafumu oipa anapangitsa mtundu wa Isiraeli kupanduka na kuyamba kulambila mafano. Pa nthawi imeneyo, aneneli a Yehova ambili okhulupilika anazunzidwa na kuphedwa. Mfumukazi Yezebeli anapangitsa kuti ufumu wa kumpoto uloŵelele m’kulambila mafano. Imeneyi inali nthawi yovuta kwambili kwa Aisiraeli. Koma pakati pa Aisiraeli, panali atumiki a Yehova ambili okhulupilika. Ena a iwo anali Mfumu Yehosafati na mneneli Eliya.

M'CIGAWO CINO

PHUNZILO 44

Kacisi wa Yehova

Mulungu ayankha pempho ya Mfumu Solomo ndipo am’dalitsa m’njila zambili.

PHUNZILO 45

Ufumu Ugaŵika

Aisiraeli ambili asiya kulambila Yehova.

PHUNZILO 46

Mulungu Woona Adziŵika pa Phili la Karimeli

Kodi Mulungu woona n’ndani? Yehova kapena Baala?

PHUNZILO 47

Yehova Alimbikitsa Eliya

Kodi uganiza kuti na iwe angakulimbikitse?

PHUNZILO 48

Mwana wa Mkazi Wamasiye Aukitsidwa

Zozizwitsa ziŵili m’nyumba imodzi!

PHUNZILO 49

Mfumukazi Yoipa Inalangiwa

Yezebeli akonza zakupha Mwisiraeli wina dzina lake Naboti, n’colinga cofuna kutenga munda wake wampesa! Kuipa komanso kupanda cilungamo kwake, Yehova Mulungu wakuona.

PHUNZILO 50

Yehova Anateteza Yehosafati

Yehosafati mfumu yabwino ipemphela kwa Mulungu pamene Ayuda awopsezedwa na mitundu yodana nawo.