Mawu Oyamba a Cigawo 8
Yehova anadalitsa Solomo mwa kum’patsa nzelu zoculuka, na mwayi womanga kacisi. Koma m’kupita kwa nthawi, iye anasiya Yehova. Ngati ndimwe kholo, m’fotokozeleni mwana wanu zimene zinapangitsa Solomo kuti asiye Mulungu. Ufumu unagaŵika, ndipo mafumu oipa anapangitsa mtundu wa Isiraeli kupanduka na kuyamba kulambila mafano. Pa nthawi imeneyo, aneneli a Yehova ambili okhulupilika anazunzidwa na kuphedwa. Mfumukazi Yezebeli anapangitsa kuti ufumu wa kumpoto uloŵelele m’kulambila mafano. Imeneyi inali nthawi yovuta kwambili kwa Aisiraeli. Koma pakati pa Aisiraeli, panali atumiki a Yehova ambili okhulupilika. Ena a iwo anali Mfumu Yehosafati na mneneli Eliya.
M'CIGAWO CINO
PHUNZILO 44
Kacisi wa Yehova
Mulungu ayankha pempho ya Mfumu Solomo ndipo am’dalitsa m’njila zambili.
PHUNZILO 46
Mulungu Woona Adziŵika pa Phili la Karimeli
Kodi Mulungu woona n’ndani? Yehova kapena Baala?
PHUNZILO 49
Mfumukazi Yoipa Inalangiwa
Yezebeli akonza zakupha Mwisiraeli wina dzina lake Naboti, n’colinga cofuna kutenga munda wake wampesa! Kuipa komanso kupanda cilungamo kwake, Yehova Mulungu wakuona.
PHUNZILO 50
Yehova Anateteza Yehosafati
Yehosafati mfumu yabwino ipemphela kwa Mulungu pamene Ayuda awopsezedwa na mitundu yodana nawo.