CIGAWO 6
Kucilikiza Ufumu —Kumanga Malo Olambilila ndi Kupeleka Thandizo Pakacitika Ngozi
TAYELEKEZELANI kuti mwaloŵa m’Nyumba ya Ufumu, ndipo mukuona kuti m’katimo mwasithilatu. Nyumba ya Ufumu imeneyi mumainyadila. Mumakumbukila nthawi imene munagwila nao nchito yomanga Nyumba ya Ufumu imeneyi mokondwa zaka zingapo zapitazo. Koma tsopano mwapeza cifukwa cina cokhalila wonyadila kwambili ndi Nyumba ya Ufumu imeneyi. Zili conco cifukwa nyumbayo aisandutsa malo ogaŵilapo thandizo la anthu amene akhudzidwa ndi ngozi yacilengedwe. Posacedwapa, kudela kwanuko kunagwa cimvula camkuntho. Madzi anasefukila, ndipo zinthu zambili zinaonongeka. Zitatelo, Komiti ya Nthambi inapanga makonzedwe akuti apezele okhudzidwawo cakudya, zovala, madzi abwino, ndi zina zofunikila. Ndipo katunduyo walongedwa mwadongosolo kwambili mu holomo. Abale ndi amene anapeleka copeleka ca katunduyo. Abale ndi alongo aima pa mzela, ndipo akulandila zinthu zimene akufunikila. Ambili mwa io akugwetsa misozi ya cimwemwe.
Yesu anakamba kuti cizindikilo cacikulu codziŵila anthu ake cidzakhala cikondi cao pa wina ndi mnzake. (Yoh. 13:34, 35) M’cigawo cino, tidzaona mmene Mboni za Yehova zimaonetselana cikondi pa nthawi yomanga malo olambilila kapena pakacitika ngozi. Cikondi cimeneci ndi umboni wakuti tikutsogoleledwa ndi Yesu yemwe ndi mfumu.
M'CIGAWO CINO
NKHANI 18
Mmene Timapezela Ndalama Zoyendetsela Nchito Za Ufumu
Kodi ndalama zimacokela kuti? Nanga zimagwila nchito yanji?
NKHANI 19
Nchito Yomanga Imene Imalemekeza Yehova
Malo olambilila amalemekeza Mulungu. Koma pali cinthu cina cimene iye amaona kuti n’cofunika kwambili.
NKHANI 20
Utumiki Wopeleka Thandizo Pakacitika Ngozi
Timadziŵa bwanji kuti nchito yopeleka thandizo pakacitika ngozi ndi mbali ya utumiki wathu wopatulika kwa Yehova?