Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

DZIKOLI LILI PA MAVUTO AAKULU

1 | Tetezani Thanzi Lanu

1 | Tetezani Thanzi Lanu

CIFUKWA CAKE KUCITA ZIMENEZI N’KOFUNIKA

Mavuto akhoza kuwononga thanzi lathu m’njila zambili.

  • Tikakumana na mavuto aakulu timapanikizika. Ndipo kupanikizika maganizo kwa nthawi yaitali kukhoza kutidwalitsa.

  • Pakagwa matsoka kapena pakacitika mavuto ena aakulu, cimakhala covuta acipatala kupeleka cithandizo cofunikila cifukwa odwala amaculuka ndipo mankhwala akhoza kucepa.

  • Matsoka amabweletsa mavuto a zacuma. Pa cifukwa cimeneci, anthu amalephela kugula zinthu zofunikila monga cakudya copatsa thanzi komanso mankhwala.

Zimene Muyenela Kudziŵa

  • Matenda aakulu komanso kupanikizika maganizo zingacititse kuti mupange zisankho zolakwika. Ndipo zimenezi zingakulepheletseni kusamalila thanzi lanu. Zotulukapo zake, matenda anu akhoza kukulilakulila.

  • Kusasamalila thanzi lanu kungapangitse kuti mudwale kwambili, ndipo zimenezi zingaike moyo wanu paciopsezo.

  • Mukakhala athanzi, m’pamenenso mumakhala okonzeka kupanga zisankho zabwino mukakumana na mavuto.

  • Kaya ndinu olemela kapena osauka, pali zimene mungacite kuti muteteze thanzi lanu.

Zimene Mungacite Pali Pano

Nthawi zonse munthu wanzelu, amaonelatu zimene zingacititse ngozi na kucita zonse zotheka kuti apewe ngoziyo. Mfundo imeneyi igwilanso pa nkhani ya thanzi lathu. Ngati timakhala aukhondo nthawi zonse, tingacepetseko kufalikila kwa matenda. Paja amati kupewa kumaposa kuciza.

“Tikakhala aukhondo komanso tikamasunga malo athu okhala ali aukhondo, timacepetsako ndalama zolipilila ku cipatala komanso zogulila mankhwala.”—Andreas. a

a Maina ena mu Galamuka! ino asinthidwa.