Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Mau oyamba

Mau oyamba

Zinsinsi 12 za Mabanja Acimwemwe

Timamva zifukwa zosiyana-siyana zimene zimapangitsa mabanja kupasuka.

  • M’zaka za pakati pa 1990 ndi 2015, ciŵelengelo ca osudzulana ku America cinawonjezeka kuwilikiza kaŵili kwa anthu a zaka zopitilila 50. Ndipo a zaka zopitilila 65 ciŵelengelo cawo cinawilikiza katatu.

  • Akatswili ena amalimbikitsa makolo kuti nthawi zonse aziyamikila ana awo. Enanso amakamba kuti azilanga ana awo mwamphamvu na colinga cofuna kuwathandiza. Conco, makolo sadziŵa zimene angacite.

  • Acicepele amakula, koma osadziŵa maluso ofunikila kuti akhale na umoyo wabwino.

Nanga cimathandiza mabanja ena kukhala acimwemwe n’ciani? Zoona n’zakuti . . .

  • Ukwati ungakhale wokondweletsa komanso mgwilizano wa moyo wonse.

  • Makolo angaphunzile kupeleka cilango mwacikondi kwa ana awo.

  • Acicepele angaphunzile maluso amene angafunikile akadzakula.

Motani? Magazini ino ya Galamuka! idzafotokoza zinsinsi 12 za mabanja acimwemwe.