Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Mafumu Aŵili Olimbana M’nthawi Yamapeto

Mafumu Aŵili Olimbana M’nthawi Yamapeto

Maulosi ena m’chati ino akamba zinthu zimene zinacitika panthawi yofanana. Maulosi onsewa amatsimikizila kuti tikukhala ‘m’nthawi yamapeto.’​—Dan. 12:4.

  • (Ma)lemba Chiv. 11:7; 12:13, 17; 13:1-8, 12

    Ulosi “Cilombo” cakhala cikulamulila padzikoli kwa zaka zoposa 3,000. M’nthawi ya mapeto, mutu wa 7 wa cilomboco unavulazidwa. Pambuyo pake, mutuwo unacila ndipo “dziko lonse” lapansi linatsatila cilomboco. Satana amaseŵenzetsa cilomboci ‘pocita nkhondo ndi otsala.’

    Kukwanilitsidwa kwake Cigumula citapita, maboma a anthu otsutsana na Yehova anayamba kulamulila padzikoli. Patapita zaka zoposa 3,000, padzikoli panacitika Nkhondo Yoyamba Yapadziko Lonse. Pa nthawi ya nkhondoyo, limodzi mwa maboma amphamvu lochedwa Britain linacepa mphamvu kwambili. Boma la Britain linakhalanso lamphamvu litagwilizana na boma la America. Maka-maka m’nthawi ya mapeto ino, Satana wakhala akuseŵenzetsa maboma onse a anthu pozunza atumiki a Mulungu.

  • (Ma)lemba Dan. 11:25-45

    Ulosi Kulimbana kwa mfumu ya kumpoto na mfumu ya kum’mwela m’nthawi yamapeto.

    Kukwanilitsidwa kwake Dziko la Germany linacita nkhondo na Britain na America. Mu 1945, boma la Soviet Union na maiko ogwilizana nalo anakhala mfumu ya kumpoto. Mu 1991, boma la Soviet Union linatha, ndipo m’kupita kwa nthawi dziko la Russia na maiko ogwilizana nalo ndiwo anakhala mfumu ya kumpoto.

  • (Ma)lemba Yes. 61:1; Mal. 3:1; Luka 4:18

    Ulosi Yehova adzatumiza “mthenga” wake kuti ‘akonze njila’ Ufumu wa Mesiya usanakhazikitsidwe. Mthengayo adzalengeza “uthenga wabwino kwa anthu ofatsa.”

    Kukwanilitsidwa kwake Kuyambila m’ma 1870, M’bale C. T. Russell na anzake anali kuphunzila Baibo mwakhama kuti amvetsetse coonadi na kuuzako ena. M’zaka za m’ma 1880, iwo anayamba kulimbikitsa atumiki a Mulungu kuti azilalikila. Anafalitsa nkhani monga yakuti, “Alaliki 1,000 Akufunika,” komanso yakuti “Anadzozedwa Kuti Azilalikila.”

  • (Ma)lemba Mat. 13:24-30, 36-43

    Ulosi Munthu anafesa tiligu m’munda. Mdani anabwela na kufesamo namsongole. Namsongoleyo analoledwa kukula mpaka kuphimba tiligu. Panthawi yokolola, namsongoleyo akumucotsa pakati pa tiligu.

    Kukwanilitsidwa kwake Kuyambila mu 1870, kusiyana pakati pa Akhristu oona na Akhristu onama kunayamba kuonekela kwambili. M’nthawi ya mapeto, Akhristu oona akusonkhanitsidwa na kulekanitsidwa na Akhristu onama.

  • (Ma)lemba Dan. 2:31-33, 41-43

    Ulosi Mapazi a fano lopangidwa na zinthu zosiyana-siyana. Mapaziwo ni acitsulo cosakanizika na dongo.

    Kukwanilitsidwa kwake Dongo ni anthu wamba olamulidwa na Britain na America amene amatsutsa maboma amenewa. Anthu amenewa amapangitsa kuti ulamulilo wamphamvu padziko lonse wa Britain na America uzilephela kucita zinthu mwamphamvu mmene ungathele.

  • (Ma)lemba Mat. 13:30; 24:14, 45; 28:19, 20

    Ulosi “Tiligu” akumusonkhanitsa na kumuika “m’nkhokwe,” ndipo “kapolo wokhulupilika ndi wanzelu” anaikidwa kuti aziyang’anila anchito apakhomo. “Uthenga wabwino uwu wa ufumu” unayamba kulalikidwa “padziko lonse lapansi kumene kuli anthu.”

    Kukwanilitsidwa kwake Mu 1919, kapolo wokhulupilika anaikidwa kuti aziyang’anila anthu a Mulungu. Kuyambila pa nthawiyo, Ophunzila Baibo anawonjezela cangu cawo pa nchito yolalikila. Masiku ano, Mboni za Yehova zimalalikila m’maiko oposa 200, ndiponso zimafalitsa mabuku ophunzilila Baibo m’vitundu voposa 1,000.

  • (Ma)lemba Dan. 12:11; Chiv. 13:11, 14, 15

    Ulosi Cilombo ca nyanga ziŵili cinauza anthu “kupanga cifanizilo ca cilombo” ca mitu 7 komanso cinapeleka ‘mpweya ku cifaniziloco.’

    Kukwanilitsidwa kwake Ulamulilo wamphamvu padziko lonse wa Britain na America unayambitsa bungwe la League of Nations. Maiko enanso anayamba kucilikiza bungweli. M’kupita kwa nthawi, mfumu ya kumpoto nayonso inaloŵa m’bungweli. Koma inangokhalamo kuyambila mu 1926 mpaka mu 1933. Anthu anali kukhulupilila kuti bungwe la League of Nations lidzabweletsa mtendele padziko lonse, pamene m’ceni-ceni ni Ufumu wa Mulungu wokha ungacite zimenezi. Masiku ano, anthu amakhulupililanso kuti United Nations idzabweletsa mtendele padziko lonse.

  • Lemba Dan. 8:​23, 24

    Ulosi Mfumu ya maonekedwe oopsa “idzawononga zinthu zambili.”

    Kukwanilitsidwa kwake Ulamulilo Wamphamvu Padziko Lonse wa Britain na America unapha anthu ambili komanso unawononga zinthu zambili. Mwacitsanzo, pa Nkhondo Yaciŵili ya Padziko Lonse, dziko la America linaponya mabomba aŵili a nyukiliya m’dziko lodana na Britain na America. Mabombawo anapha anthu ambili komanso anawononga zinthu zoculuka kuposa cida cina ciliconse.

  • (Ma)lemba Dan. 11:31; Chiv. 17:​3, 7-11

    Ulosi ‘Cilombo cofiila kwambili’ cokhala na nyanga 10 cinatuluka m’phompho, ndipo ndico mfumu ya 8. Buku la Danieli limachula mfumu imeneyi kuti “cinthu conyansa cobweletsa ciwonongeko.”

    Kukwanilitsidwa kwake Mkati mwa Nkhondo Yaciŵili ya Padziko Lonse Bungwe la League of Nations linaleka kugwila nchito. Nkhondoyo itatha, bungwe la United Nations ‘linaikidwa pamalowo,’ kapena kuti linakhazikitsidwa. Mofanana na League of Nations, bungwe la United Nations limapatsidwa ulemelelo woyenela kupelekedwa ku Ufumu wa Mulungu. Bungweli lidzaukila zipembedzo zonama.

  • (Ma)lemba 1 Ates. 5:3; Chiv. 17:16

    Ulosi Atsogoleli a maiko adzalengeza “Bata ndi mtendele!” Kenako “nyanga 10” komanso “cilombo,” zidzaukila “hulelo” na kuliwononga. Pambuyo pake, mitundu ya anthu idzawonongedwa.

    Kukwanilitsidwa kwake Atsogoleli a maiko adzalengeza kuti akwanitsa kubweletsa bata na mtendele padzikoli. Ndiyeno, maiko amene amacilikiza bungwe la United Nations adzawononga zipembedzo zonama. Ici cidzakhala ciyambi ca cisautso cacikulu. Cisautso cacikulu cidzatha pamene Yesu adzawononga mbali yotsala ya dziko la Satana pa Aramagedo.

  • (Ma)lemba Ezek. 38:11, 14-17; Mat. 24:31

    Ulosi Gogi adzaukila dziko la anthu a Mulungu. Ndiyeno, angelo adzasonkhanitsa anthu “osankhidwa.”

    Kukwanilitsidwa kwake Mfumu ya kumpoto pamodzi na maboma ena onse adzaukila anthu a Mulungu. Panthawi inayake kuukilako kuli mkati, otsalila odzozedwa adzatengedwa kupita kumwamba.

  • (Ma)lemba Ezek. 38:18-23; Dan. 2:34, 35, 44, 45; Chiv. 6:2; 16:14, 16; 17:14; 19:20

    Ulosi ‘Wokwela’ pa “hachi yoyela” adzatsiliza ‘kugonjetsa adani ake’ mwa kuwononga Gogi na gulu lake la nkhondo. “Cilombo” ‘cidzaponyedwa m’nyanja ya moto,’ komanso cifanizilo cacikulu cidzaphwanyidwa-phwanyidwa.

    Kukwanilitsidwa kwake Yesu, Mfumu ya Ufumu wa Mulungu, adzabwela kudzapulumutsa anthu a Mulungu. Iye pamodzi na olamulila anzake 144,000, komanso magulu ankhondo a angelo, adzawononga mitundu yonse ya anthu oukila anthu a Mulungu. Uku ndiye kudzakhala kutha kwa dziko la Satana.