NYIMBO 153
Nilimbitseni Mtima
(2 Mafumu 6:16)
1. Navutika mtima—
Nasoŵa cocita.
Olo zinthu zinivute;
Mumanithandiza.
Moyo ungavute,
Koma nimadziŵa:
Ndimwe wokhulupilika;
Mudzaniteteza.
(KOLASI)
Yehova, nithandizeni
Kuti niziona.
Tilidi ambili kuposa
Olimbana nafe.
Conde, n’thandizeni
Kuti nipilile.
Nilimbitseni mtima,
Simungalephele.
2. Ndine cabe munthu.
Nimacita mantha.
Ndimwe pothaŵila panga;
Simumalephela.
Munipatse mphamvu,
Kuti nisayope.
Ine nidzapililabe—
Kufikila imfa.
(KOLASI)
Yehova, nithandizeni
Kuti niziona.
Tilidi ambili kuposa
Olimbana nafe.
Conde, n’thandizeni
Kuti nipilile.
Nilimbitseni mtima,
Simungalephele.
(KOLASI)
Yehova, nithandizeni
Kuti niziona.
Tilidi ambili kuposa
Olimbana nafe.
Conde, n’thandizeni
Kuti nipilile.
Nilimbitseni mtima,
Simungalephele.
Nilimbitseni mtima,
Simungalephele.