Kalata Yoyamba Yopita kwa Akorinto 10:1-33

  • Zitsanzo zotichenjeza za Aisiraeli (1-13)

  • Chenjezo pa nkhani yolambira mafano (14-22)

    • Tebulo la Yehova ndiponso tebulo la ziwanda (21)

  • Ufulu ndiponso kuganizira ena (23-33)

    • “Muzichita zinthu zonse kuti zibweretse ulemerero kwa Mulungu” (31)

10  Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti makolo athu akale, onse anali pansi pa mtambo+ ndipo onse anawoloka nyanja.+  Onse anabatizidwa mwa Mose, kudzera mu mtambo ndi nyanja.  Onse ankadya chakudya chauzimu chofanana.+  Ndipo onse ankamwa madzi auzimu ofanana.+ Chifukwa ankamwa pathanthwe lauzimu limene linkawatsatira, ndipo thanthwelo linali* Khristu.+  Ngakhale zinali choncho, ambiri a iwo Mulungu sanakondwere nawo ndipo anaphedwa mʼchipululu.+  Zinthu zimenezi ndi zitsanzo kwa ife, kuti nafenso tisamalakelake zinthu zoipa ngati mmene iwo anachitira.+  Ndipo tisamalambire mafano ngati mmene ena a iwo anachitira, mogwirizana ndi zimene Malemba amanena kuti: “Anthu anakhala pansi ndipo anadya ndi kumwa. Kenako anaimirira nʼkuyamba kusangalala.”+  Komanso tisamachite chiwerewere,* mmene ena a iwo anachitira, nʼkufa anthu 23,000 tsiku limodzi.+  Tisamamuyesenso Yehova,* mmene ena a iwo anamuyesera,+ nʼkufa atalumidwa ndi njoka.+ 10  Tisakhalenso ongʼungʼudza, ngati mmene ena a iwo anachitira,+ nʼkuphedwa ndi mngelo wowononga.+ 11  Zinthu zimene zinawachitikirazi ndi zitsanzo kwa ife ndipo zinalembedwa kuti zitichenjeze ifeyo+ amene tikukhala kumapeto a nthawi ino. 12  Choncho amene akuganiza kuti waima bwinobwino asamale kuti asagwe.+ 13  Palibe mayesero amene mwakumana nawo osiyana ndi amene anthu ena amakumana nawo.+ Koma Mulungu ndi wokhulupirika ndipo sadzalola kuti muyesedwe kufika pamene simungapirire,+ koma pamene mukukumana ndi mayeserowo iye adzapereka njira yopulumukira kuti muthe kuwapirira.+ 14  Choncho okondedwa anga, pewani* kulambira mafano.+ 15  Ndikulankhula nanu ngati anthu ozindikira. Weruzani nokha ngati zimene ndikunenazi nʼzoona. 16  Kodi kapu ya madalitso imene timadalitsa, sitanthauza kugawana magazi a Khristu?+ Kodi mkate umene timaugawagawa, sutanthauza kugawana thupi la Khristu?+ 17  Popeza pali mkate umodzi, ifeyo, ngakhale kuti tilipo ambiri, ndife thupi limodzi,+ chifukwa tonse tikudya nawo mkate umodziwo. 18  Taganizirani zimene Aisiraeli* amachita: Kodi amene amadya zinthu zoperekedwa paguwa la nsembe si ndiye kuti amakhala ngati akudya ndi Mulungu?+ 19  Kodi mfundo yake ndi yotani? Kodi zinthu zoperekedwa nsembe kwa mafano kapena mafano enieniwo ndi kanthu? 20  Ayi, koma ndikutanthauza kuti zinthu zimene anthu a mitundu ina amapereka nsembe amazipereka kwa ziwanda, osati kwa Mulungu.+ Ndipo sindikufuna kuti muzichita chilichonse chogwirizana ndi ziwanda.+ 21  Sizingatheke kuti muzimwa zamʼkapu ya Yehova* komanso zamʼkapu ya ziwanda. Sizingathekenso kuti muzidya “patebulo la Yehova”*+ komanso patebulo la ziwanda. 22  Kapena ‘kodi tikufuna kuti Yehova* achite nsanje?’+ Kodi mphamvu zathu zingapose mphamvu zake? 23  Zinthu zonse nʼzololeka, koma si zonse zimene zili zaphindu. Zinthu zonse nʼzololeka, koma si zonse zomwe zimalimbikitsa.+ 24  Aliyense asamangofuna zopindulitsa iyeyo basi, koma zopindulitsanso ena.+ 25  Muzidya chilichonse chogulitsidwa pamsika wa nyama muli ndi chikumbumtima chabwino ndipo musafunse mafunso. 26  Chifukwa “dziko lapansi ndi zonse zimene zili mmenemo ndi za Yehova.”*+ 27  Ngati munthu wosakhulupirira wakuitanani ndipo mukufuna kupita, kadyeni chilichonse chimene wakupatsani muli ndi chikumbumtima chabwino ndipo musafunse mafunso. 28  Koma wina akakuuzani kuti: “Izi zaperekedwa nsembe,” musadye zimenezo kuopera amene wakuuzaniyo ndiponso chikumbumtima.+ 29  Sindikunena chikumbumtima chako, koma cha munthu winayo. Sindikufuna kuti ndizigwiritsa ntchito ufulu wanga kenako nʼkumaweruzidwa ndi chikumbumtima cha munthu wina.+ 30  Ngakhale nditakhala ndi ufulu wodya chakudyacho nʼkuyamika Mulungu, kodi ndi bwino kuchita zimenezo ngati zingachititse kuti anthu ena andinyoze?+ 31  Choncho kaya mukudya kapena kumwa, kapena kuchita china chilichonse, muzichita zinthu zonse kuti zibweretse ulemerero kwa Mulungu.+ 32  Muzipewa kukhumudwitsa Ayuda, Agiriki ndiponso mpingo wa Mulungu.+ 33  Zimenezi ndi zimene inenso ndikuyesetsa kuchita. Ndikuyesetsa kusangalatsa anthu onse pa zonse zimene ndikuchita. Sindikufuna zopindulitsa ine ndekha,+ koma zopindulitsa anthu ambiri kuti apulumutsidwe.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “linkatanthauza.”
MʼChigiriki por·nei′a. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Kapena kuti, “thawani.”
Kapena kuti, “Aisiraeli akuthupi.”