1 Mafumu 1:1-53

  • Davide ndi Abisagi (1-4)

  • Adoniya ankafuna kukhala mfumu (5-10)

  • Zimene anachita Natani ndi Bati-seba (11-27)

  • Davide analamula kuti Solomo adzozedwe kukhala mfumu (28-40)

  • Adoniya anathawira kuguwa la nsembe (41-53)

1  Mfumu Davide anakalamba+ ndipo anali ndi zaka zambiri. Ankamufunditsa zofunda koma sankamva kutentha.  Choncho atumiki ake anamuuza kuti: “Mbuyathu mfumu, bwanji tikufunireni mtsikana yemwe ndi namwali woti azikusamalirani? Azigona pafupi nanu kuti inu mbuyathu mfumu muzimva kutentha.”  Ndiyeno anafufuza mtsikana wokongola mʼdziko lonse la Isiraeli. Kenako anapeza Abisagi+ wa ku Sunemu+ ndipo anabwera naye kwa mfumu.  Mtsikanayo anali chiphadzuwa ndipo ankasamalira mfumu. Koma mfumuyo sinagonepo naye.  Pa nthawi imeneyi Adoniya+ mwana wa Hagiti anayamba kudzikweza nʼkumanena kuti: “Ineyo ndikhala mfumu!” Iye anapangitsa galeta ndipo anali ndi amuna okwera pamahatchi* komanso amuna 50 oti azithamanga patsogolo pake.+  Koma bambo ake sanamʼdzudzulepo* nʼkumufunsa kuti: “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Iye analinso wooneka bwino kwambiri ndipo mayi ake anamʼbereka pambuyo pobereka Abisalomu.  Iye anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya komanso wansembe Abiyatara+ ndipo awiriwa anayamba kumutsatira komanso kumuthandiza.+  Koma wansembe Zadoki,+ Benaya+ mwana wa Yehoyada, mneneri Natani,+ Simeyi,+ Reyi ndi amuna amphamvu a Davide+ sanagwirizane ndi Adoniya.  Kenako Adoniya anapereka nsembe+ za nkhosa, ngʼombe komanso ana a ngʼombe onenepa pafupi ndi mwala wa Zoheleti womwe uli pafupi ndi Eni-rogeli. Anaitana azichimwene ake onse omwe anali ana a mfumu komanso amuna onse a mu Yuda omwe anali atumiki a mfumu. 10  Koma sanaitane mneneri Natani, Benaya, asilikali amphamvu a Davide ndiponso mchimwene wake Solomo. 11  Kenako Natani+ anauza Bati-seba+ mayi ake a Solomo+ kuti: “Kodi mwamva zoti Adoniya,+ mwana wa Hagiti, wakhala mfumu koma mbuye wathu Davide sakudziwa chilichonse? 12  Tsopano mvetserani malangizo amene ndikufuna kukupatsani, kuti mupulumutse moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomo.+ 13  Mupite kwa Mfumu Davide mukanene kuti, ‘Kodi si inu mbuyanga mfumu amene munalumbirira ine kapolo wanu kuti: “Solomo mwana wako ndi amene adzakhale mfumu pambuyo panga, ndipo iye ndi amene adzakhale pampando wanga wachifumu”?+ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya wakhala mfumu?’ 14  Inu mukamakalankhula ndi mfumuyo, ineyo ndidzabwera kudzatsimikizira zimene mukunena.” 15  Zitatero, Bati-seba anapita kuchipinda kumene kunali mfumu. Mfumuyo inali yokalamba kwambiri ndipo Abisagi+ wa ku Sunemu ankaisamalira. 16  Bati-seba anagwada nʼkuweramira mfumu ndipo mfumuyo inati: “Ukufuna kupempha chiyani?” 17  Bati-seba anayankha kuti: “Mbuyanga, ndinu amene munalumbira mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kwa ine kapolo wanu kuti, ‘Mwana wako Solomo ndi amene adzakhale mfumu pambuyo panga ndipo iye ndi amene adzakhale pampando wanga wachifumu.’+ 18  Koma tsopano Adoniya wakhala mfumu ndipo inu mbuyanga mfumu simukudziwa chilichonse.+ 19  Iye wapereka nsembe zambiri za ngʼombe zamphongo, nyama zonenepa ndiponso nkhosa. Komanso waitana ana onse a mfumu, wansembe Abiyatara ndi Yowabu mkulu wa asilikali,+ koma mtumiki wanu Solomo sanamuitane.+ 20  Panopa maso a Aisiraeli onse ali pa inu mbuyanga mfumu, kuti muwauze amene akhale pampando wanu wachifumu pambuyo panu. 21  Mukapanda kutero, inuyo mbuyanga mfumu mukadzangogona mʼmanda mofanana ndi makolo anu, ineyo ndi mwana wanga Solomo tidzaonedwa ngati oukira.” 22  Bati-seba akulankhula ndi mfumuyo, mneneri Natani analowa.+ 23  Nthawi yomweyo anthu anauza mfumu kuti: “Kwabwera mneneri Natani!” Kenako Natani anagwada nʼkuweramira mfumuyo mpaka nkhope yake kufika pansi. 24  Ndiyeno Natani anati: “Mbuyanga mfumu, kodi munanena kuti, ‘Adoniya adzakhala mfumu pambuyo panga ndipo ndi amene adzakhale pampando wanga wachifumuʼ?+ 25  Chifukwatu lero wapita kukapereka nsembe+ zambiri za ngʼombe zamphongo, nyama zonenepa ndi nkhosa. Waitananso ana onse a mfumu, atsogoleri a asilikali komanso wansembe Abiyatara.+ Moti panopa ali kumeneko ndipo akudya ndi kumwa naye nʼkumanena kuti, ‘Mfumu Adoniya ikhale ndi moyo wautali!’ 26  Koma sanaitane ineyo mtumiki wanu, wansembe Zadoki, Benaya+ mwana wa Yehoyada komanso Solomo mtumiki wanu. 27  Kodi inuyo mbuyanga mfumu mwalamula zimenezi osandidziwitsa ine mtumiki wanu, kuti ndi ndani amene adzakhale pampando wanu wachifumu pambuyo panu?” 28  Zitatero Mfumu Davide inati: “Tamuitaneni Bati-seba.” Choncho Bati-seba anabwera nʼkuima pamaso pa mfumu. 29  Mfumuyo inalumbira kuti: “Mʼdzina la Yehova amene anandipulumutsa mʼmasautso onse,+ 30  zimene ndinakulumbirira mʼdzina la Yehova Mulungu wa Isiraeli kuti, ‘Mwana wako Solomo adzakhala mfumu pambuyo panga ndipo iye ndi amene adzakhale pampando wanga wachifumu mʼmalo mwanga,’ ndi zimene ndichite lero.” 31  Kenako Bati-seba anagwada nʼkuweramira mfumu mpaka nkhope yake kufika pansi ndipo ananena kuti: “Mbuyanga Mfumu Davide, mukhale ndi moyo mpaka kalekale!” 32  Nthawi yomweyo Mfumu Davide inati: “Ndiitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya+ mwana wa Yehoyada.”+ Ndipo anthuwo anabweradi. 33  Mfumuyo inawauza kuti: “Tengani atumiki a mbuye wanu nʼkukweza Solomo mwana wanga panyulu* yanga,+ ndipo mupite naye ku Gihoni.+ 34  Kumeneko, wansembe Zadoki ndi mneneri Natani akamudzoze+ kukhala mfumu ya Isiraeli. Ndiyeno mukalize lipenga nʼkunena kuti, ‘Mfumu Solomo akhale ndi moyo wautali!’+ 35  Ndiye pobwera muzikamulondola, ndipo adzafike kuno nʼkukhala pampando wanga wachifumu. Iyeyo adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo ndidzamuika kukhala mtsogoleri wa Isiraeli ndi Yuda.” 36  Nthawi yomweyo Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti: “Ame!* Yehova, Mulungu wa mbuyanga mfumu, atsimikizire zimenezi. 37  Mmene Yehova anakhalira ndi inu mbuyanga mfumu, akhalenso ndi Solomo+ ndipo achititse mpando wake wachifumu kukhala waukulu kuposa mpando wanu wachifumu, mbuyanga Mfumu Davide.”+ 38  Kenako wansembe Zadoki, mneneri Natani, Benaya+ mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti+ anapita kukakweza Solomo panyulu ya Mfumu Davide+ nʼkupita naye ku Gihoni.+ 39  Ndiyeno wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta+ mutenti+ nʼkudzoza Solomo.+ Zitatero anthuwo anayamba kuliza lipenga nʼkumafuula kuti: “Mfumu Solomo akhale ndi moyo wautali!” 40  Atatero anthuwo anayamba kumulondola ndipo ankaimba zitoliro akusangalala kwambiri, moti nthaka inangʼambika chifukwa cha phokoso lawo.+ 41  Adoniya ndi anthu onse amene anawaitana anamva phokosolo, ndipo anali atangomaliza kudya.+ Yowabu atangomva kulira kwa lipenga anafunsa kuti: “Kodi phokoso likumveka mumzindali ndi la chiyani?” 42  Asanamalize kulankhula, kunabwera Yonatani+ mwana wa wansembe Abiyatara. Ndipo Adoniya anati: “Lowa, iwe ndiwe munthu wabwino ndipo uyenera kuti wabweretsa nkhani yabwino.” 43  Koma Yonatani anayankha Adoniya kuti: “Ayi, si nkhani yabwino! Mbuyathu Mfumu Davide wapatsa Solomo ufumu. 44  Mfumu inatuma wansembe Zadoki, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ndipo iwo anakweza Solomo panyulu ya mfumu.+ 45  Kenako wansembe Zadoki ndi mneneri Natani anakamudzoza ufumu ku Gihoni. Ndiyeno abwerako akusangalala ndipo mumzinda muli phokoso lokhalokha. Phokoso limenelo ndi limene munamva lija. 46  Panopa, Solomo wakhala pampando wachifumu. 47  Kuwonjezera apo, atumiki a mfumu abwera kudzafunira mafuno abwino mbuye wathu Mfumu Davide kuti: ‘Mulungu wanu akulitse dzina la Solomo kuposa dzina lanu ndiponso akweze ufumu wake kuposa ufumu wanu!’ Kenako mfumuyo inaweramitsa mutu wake ili pabedi. 48  Komanso mfumu inanena kuti, ‘Atamandike Yehova Mulungu wa Isiraeli, amene lero wapereka munthu woti akhale pampando wanga wachifumu, ndipo walola kuti maso anga aone zimenezi.’” 49  Anthu onse amene anaitanidwa ndi Adoniya anachita mantha ndipo ananyamuka nʼkumapita. 50  Nayenso Adoniya anachita mantha ndi Solomo. Choncho anapita kukagwira nyanga za guwa lansembe.+ 51  Solomo anauzidwa kuti: “Adoniya akuchita mantha ndi inu Mfumu Solomo moti wakagwira nyanga za guwa lansembe, ndipo wanena kuti, ‘Mfumu Solomo andilumbirire kaye ine mtumiki wake kuti sandipha ndi lupanga.’” 52  Solomo anayankha kuti: “Akamachita zabwino, tsitsi lake ngakhale limodzi silidzagwera pansi, koma akadzapezeka atachita choipa,+ adzaphedwa.” 53  Choncho Mfumu Solomo inatumiza anthu kuti akatenge Adoniya paguwa lansembe nʼkubwera naye. Kenako Adoniya analowa nʼkugwadira Mfumu Solomo. Ndiyeno Solomo anamuuza kuti: “Pita kunyumba kwako.”

Mawu a M'munsi

Ena amati “mahosi.”
Kapena kuti, “sanafune kumukhumudwitsa.”
“Nyulu” ndi nyama yooneka ngati hatchi.
Kapena kuti, “Zikhale momwemo!”