1 Mafumu 12:1-33

  • Rehobowamu sanayankhe bwino anthu (1-15)

  • Mafuko 10 anagalukira Solomo (16-19)

  • Yerobowamu anakhala mfumu ya Isiraeli (20)

  • Rehobowamu anamuletsa kuti asakamenyane ndi Aisiraeli (21-24)

  • Yerobowamu anayamba kulambira mwana wa ngʼombe (25-33)

12  Rehobowamu anapita ku Sekemu+ chifukwa Aisiraeli onse anapita kumeneko kuti akamuveke ufumu.+  Yerobowamu mwana wa Nebati anamva zimenezi ali ku Iguputo, (iye anali ku Iguputo chifukwa anathawa Mfumu Solomo nʼkukakhala kumeneko),+  ndipo anthu anatumiza uthenga womuitana. Kenako Yerobowamu ndi gulu lonse la Aisiraeli anabwera kwa Rehobowamu nʼkumuuza kuti:  “Bambo anu anachititsa kuti goli lathu likhale lowawa.+ Koma inuyo mukatifewetsera ntchito yowawa ya bambo anu komanso goli lolemera limene ankatisenzetsa, tizikutumikirani.”  Rehobowamu atamva zimenezi anauza anthuwo kuti: “Pitani kaye ndipo mukabwerenso pakatha masiku atatu.” Choncho anthuwo anapitadi.+  Ndiyeno Mfumu Rehobowamu anafunsa nzeru kwa anthu achikulire* amene ankatumikira bambo ake Solomo pamene anali moyo. Anawafunsa kuti: “Kodi mukuganiza kuti anthuwa ndiwayankhe bwanji?”  Iwo anamuuza kuti: “Ngati lero mungakhale mtumiki wa anthuwa, kumvera zimene apempha ndiponso kuwayankha bwino, iwo adzakhala atumiki anu nthawi zonse.”  Koma iye sanamvere malangizo amene anthu achikulirewo* anamupatsa, ndipo anapita kukafunsira malangizo kwa achinyamata amene anakulira naye limodzi, omwe ankamutumikira.+  Iye anawafunsa kuti: “Kodi mukuganiza kuti tiwayankhe bwanji anthuwa, amene andiuza kuti, ‘Mutifewetsere goli limene bambo anu anatisenzetsaʼ?” 10  Achinyamata amene anakulira naye limodziwo anamuuza kuti: “Anthu amene akuuzani kuti, ‘Bambo anu anatisenzetsa goli lolemera, koma inuyo mutipeputsirekoʼ mukawauze kuti, ‘Chala changa chachingʼono chidzakhala chachikulu kuposa chiuno cha bambo anga. 11  Bambo anga anakusenzetsani goli lolemera koma ineyo ndiwonjezera goli lanulo. Bambo anga ankakukwapulani ndi zikwapu koma ineyo ndizikukwapulani ndi zikoti zaminga.’” 12  Pa tsiku lachitatu, Yerobowamu ndi anthu onse anapita kwa Rehobowamu, mogwirizana ndi zimene mfumuyo inanena kuti: “Mukabwerenso pakatha masiku atatu.”+ 13  Koma mfumuyo inayankha anthuwo mwaukali ndipo sinamvere malangizo a anthu achikulire* aja. 14  Inayankha anthuwo motsatira malangizo a achinyamata aja. Inati: “Bambo anga anakusenzetsani goli lolemera koma ineyo ndiwonjezera goli lanulo. Bambo anga ankakukwapulani ndi zikwapu koma ineyo ndizikukwapulani ndi zikoti zaminga.” 15  Choncho mfumu sinamvere anthuwo. Yehova ndi amene anachititsa kuti zinthu zikhale chonchi,+ kuti akwaniritse mawu amene Yehovayo analankhula kwa Yerobowamu mwana wa Nebati kudzera mwa Ahiya+ wa ku Silo. 16  Aisiraeli onse ataona kuti mfumuyo yakana kuwamvera, anayankha kuti: “Ife Davide tilibe naye ntchito ndipo sitingapatsidwe cholowa kuchokera kwa mwana wa Jese. Aisiraeli inu, aliyense apite kwa milungu yake! Tsopano iwe Davide, uziyangʼanira nyumba yako yokha.” Aisiraeliwo atatero, aliyense anabwerera kunyumba* kwawo.+ 17  Koma Rehobowamu anapitiriza kulamulira Aisiraeli amene ankakhala mʼmizinda ya ku Yuda.+ 18  Kenako Mfumu Rehobowamu inatumiza Adoramu+ amene ankayangʼanira anthu ogwira ntchito yokakamiza, koma Aisiraeli onse anamugenda ndi miyala nʼkumupha. Komabe, Mfumu Rehobowamu inatha kukwera galeta lake nʼkuthawira ku Yerusalemu.+ 19  Ndipo Aisiraeli akupitiriza kuukira+ nyumba ya Davide mpaka lero. 20  Aisiraeli onse atangomva kuti Yerobowamu wabwera, anatumiza uthenga womuitanira kumene anasonkhana, ndipo anamuika kukhala mfumu ya Aisiraeli onse.+ Palibenso amene ankatsatira nyumba ya Davide kupatulapo fuko la Yuda.+ 21  Rehobowamu atangofika ku Yerusalemu, anasonkhanitsa asilikali ophunzitsidwa bwino* okwana 180,000 a nyumba yonse ya Yuda ndi fuko la Benjamini. Anawasonkhanitsa kuti akamenyane ndi nyumba ya Isiraeli pofuna kuti ufumu ubwerere kwa Rehobowamu mwana wa Solomo.+ 22  Kenako Semaya,+ munthu wa Mulungu woona, anamva mawu ochokera kwa Mulungu woona kuti: 23  “Ukauze Rehobowamu mwana wa Solomo, mfumu ya Yuda, komanso nyumba yonse ya Yuda ndi Benjamini ndiponso anthu ena onse kuti, 24  ‘Yehova wanena kuti: “Musapite kukamenyana ndi abale anu, Aisiraeli. Aliyense abwerere kunyumba chifukwa ine ndi amene ndachititsa zimenezi.”’”+ Choncho anthuwo anamvera mawu a Yehova nʼkubwerera kwawo ngati mmene Yehova ananenera. 25  Yerobowamu anamanga* mzinda wa Sekemu+ mʼdera lamapiri la Efuraimu nʼkumakhala kumeneko. Kenako anachoka nʼkupita kukamanga* mzinda wa Penueli.+ 26  Yerobowamu anaganiza kuti: “Tsopano ufumuwu ubwerera kunyumba ya Davide.+ 27  Anthuwa akapitiriza kupita kukapereka nsembe kunyumba ya Yehova ku Yerusalemu,+ mtima wawo udzabwerera kwa mbuye wawo Rehobowamu mfumu ya Yuda. Akatero adzandipha nʼkubwerera kwa Rehobowamu mfumu ya Yuda.” 28  Mfumuyo itakambirana ndi anthu ena inapanga ana awiri a ngʼombe agolide,+ kenako inauza anthu onse kuti: “Ndikuona kuti mukuvutika kwambiri kupita ku Yerusalemu. Ndiye ndakupangirani Mulungu uyu, amene anakutulutsani mʼdziko la Iguputo+ Aisiraeli inu.” 29  Choncho mwana wa ngʼombe wina anamuika ku Beteli+ ndipo wina anakamuika ku Dani.+ 30  Zimenezi zinachititsa kuti anthuwo achimwe+ ndipo iwo ankakafika mpaka ku Dani kukalambira mwana wa ngʼombeyo. 31  Yerobowamu anamanga nyumba zolambiriramo mʼmalo okwezeka. Ndipo anasankha anthu wamba, anthu amene sanali ana a Levi, kuti akhale ansembe.+ 32  Yerobowamu anakhazikitsa chikondwerero chofanana ndi cha ku Yuda pa tsiku la 15 la mwezi wa 8.+ Paguwa la nsembe limene analimanga ku Beteli,+ anaperekapo nsembe kwa ana a ngʼombe amene anawapanga aja ndipo ku Beteliko anasankha ansembe kuti azitumikira mʼmalo okwezeka amene anapanga. 33  Yerobowamu anapereka nsembe pa tsiku la 15 la mwezi wa 8 womwe anausankha yekha. Anapereka nsembezo paguwa limene anamanga ku Beteli. Iye anayambitsa chikondwerero choti Aisiraeli azichita ndipo anakwera paguwa kukapereka nsembe zautsi komanso nsembe zina.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “akulu.”
Kapena kuti, “akuluwo.”
Kapena kuti, “malangizo a akulu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “kumatenti.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “ochita kusankhidwa.”
Kapena kuti, “analimbitsa mpanda wa.”
Kapena kuti, “nʼkupita kukalimbitsa mpanda wa.”