1 Mafumu 16:1-34

  • Yehova anaweruza Basa (1-7)

  • Ela, mfumu ya Isiraeli (8-14)

  • Zimiri, mfumu ya Isiraeli (15-20)

  • Omuri, mfumu ya Isiraeli (21-28)

  • Ahabu, mfumu ya Isiraeli (29-33)

  • Hiyeli anamanganso Yeriko (34)

16  Yehova analankhula mawu otsutsa Basa mwana wa Haneni+ kudzera mwa Yehu,+ kuti:  “Ndinakukweza kukuchotsa pafumbi kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisiraeli.+ Koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira ya Yerobowamu nʼkuchimwitsa anthu anga Aisiraeli ndipo andikwiyitsa ndi machimo awo.+  Choncho ndidzaseseratu Basa ndi nyumba yake ndipo ndidzachititsa nyumba yake kukhala ngati nyumba ya Yerobowamu+ mwana wa Nebati.  Munthu aliyense wa mʼbanja la Basa amene adzafere mumzinda, agalu adzamudya ndipo amene adzafere kutchire, mbalame zidzamudya.”  Nkhani zina zokhudza Basa ndi zimene anachita ndiponso mphamvu zake, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Isiraeli.  Kenako Basa, mofanana ndi makolo ake, anamwalira ndipo anaikidwa mʼmanda ku Tiriza.+ Ndiyeno mwana wake Ela anakhala mfumu mʼmalo mwake.  Komanso Yehova analankhula mawu otsutsa Basa ndi nyumba yake kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Haneni. Anamutsutsa chifukwa cha zoipa zonse zimene Basayo anachita pamaso pa Yehova pomukwiyitsa ndi ntchito ya manja ake ngati mmene anthu a mʼnyumba ya Yerobowamu anachitira ndiponso chifukwa chakuti iye anapha Nadabu.+  Mʼchaka cha 26 cha Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Basa anakhala mfumu ya Isiraeli ku Tiriza ndipo analamulira zaka ziwiri.  Kenako mtumiki wake Zimiri, amene ankayangʼanira hafu ya asilikali oyenda pa magaleta, anamukonzera chiwembu pamene Ela ankamwa mowa mpaka kuledzera kunyumba ya Ariza ku Tiriza. Ariza anali woyangʼanira banja la mfumu ku Tirizako. 10  Ndiyeno Zimiri anafika nʼkupha Ela+ ndipo zimenezi zinachitika mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Kenako Zimiri anakhala mfumu mʼmalo mwake. 11  Iye atangokhala pampando wachifumu nʼkuyamba kulamulira, anapha anthu onse a mʼnyumba ya Basa. Sanasiye ndi moyo mwamuna* aliyense wa mʼbanja la Basa, kaya wachibale* wake kapena mnzake. 12  Choncho Zimiri anapha anthu onse a mʼnyumba ya Basa, mogwirizana ndi mawu a Yehova otsutsa Basa amene analankhula kudzera mwa mneneri Yehu.+ 13  Anawapha onse chifukwa cha machimo onse amene Basa ndi mwana wake Ela anachita, komanso machimo amene Aisiraeli anachita chifukwa cha iwo nʼkukwiyitsa Yehova Mulungu wa Isiraeli ndi mafano awo opanda pake.+ 14  Nkhani zina zokhudza Ela ndiponso zonse zimene anachita, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Isiraeli. 15  Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimiri anakhala mfumu ku Tiriza ndipo analamulira masiku 7. Pa nthawiyo nʼkuti asilikali atamanga msasa pafupi ndi mzinda wa Gibitoni,+ umene unali wa Afilisiti, kuti amenyane ndi anthu amumzindawo. 16  Patapita nthawi, asilikali a mumsasawo anamva kuti: “Zimiri anakonzera chiwembu mfumu ndipo waipha.” Choncho tsiku limenelo, Aisiraeli onse omwe anali kumsasako anaveka ufumu Omuri,+ mkulu wa asilikali, kuti akhale mfumu ya Isiraeli. 17  Kenako Omuri ndi Aisiraeli onse amene anali naye, anachoka ku Gibitoni nʼkupita kukaukira mzinda wa Tiriza. 18  Zimiri ataona kuti mzindawo walandidwa, anakalowa munsanja yomwe inali panyumba ya mfumu nʼkuyatsa nyumbayo iye ali momwemo, moti anafa.+ 19  Anafa chifukwa cha machimo ake popeza anachita zoipa pamaso pa Yehova, anayenda mʼnjira ya Yerobowamu komanso chifukwa cha machimo amene Aisiraeli anachita chifukwa cha iyeyo.+ 20  Nkhani zina zokhudza Zimiri ndi chiwembu chimene anakonza, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Isiraeli. 21  Pa nthawi imeneyi mʼpamene anthu a ku Isiraeli anagawikana mʼmagulu awiri. Gulu lina linkatsatira Tibini mwana wa Ginati ndipo linkafuna kumuveka ufumu ndipo gulu linalo linkatsatira Omuri. 22  Koma anthu amene ankatsatira Omuri anagonjetsa amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu. 23  Omuri anakhala mfumu ya Isiraeli mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda ndipo analamulira zaka 12. Ku Tiriza analamulirako zaka 6. 24  Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri ndi matalente* awiri asiliva ndipo anamanga mzinda paphiripo. Mzindawo anaupatsa dzina lakuti Samariya*+ lomwe linali dzina la Semeri, mwiniwake* wa phirilo. 25  Omuri anapitiriza kuchita zoipa pamaso pa Yehova ndipo anachita zoipa kwambiri kuposa mafumu onse amene anakhalapo iye asanakhale mfumu.+ 26  Iye anayenda mʼnjira zonse za Yerobowamu mwana wa Nebati komanso mʼmachimo amene Aisiraeli anachita chifukwa cha iye pokwiyitsa Yehova Mulungu wa Isiraeli ndi mafano awo opanda pake.+ 27  Nkhani zina zokhudza Omuri, zimene anachita ndiponso mphamvu zake, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Isiraeli. 28  Kenako Omuri, mofanana ndi makolo ake, anamwalira nʼkuikidwa mʼmanda ku Samariya ndipo mwana wake Ahabu+ anakhala mfumu mʼmalo mwake. 29  Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Isiraeli mʼchaka cha 38 cha Asa mfumu ya Yuda. Iye analamulira Isiraeli ku Samariya+ kwa zaka 22. 30  Ahabu mwana wa Omuri anachita zoipa kwambiri pamaso pa Yehova kuposa mafumu onse amene anakhalapo iye asanakhale mfumu.+ 31  Ngati kuti kuyenda mʼmachimo a Yerobowamu+ mwana wa Nebati kunali kosakwanira, Ahabu anakwatira Yezebeli+ mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni,+ ndipo anayamba kutumikira Baala+ nʼkumamugwadira. 32  Kuwonjezera pamenepo, anamanga guwa lansembe la Baala mʼkachisi wa Baala+ amene iye anamanga ku Samariya. 33  Ahabu anaimikanso mzati wopatulika.*+ Iye anachita zinthu zambiri zokwiyitsa Yehova Mulungu wa Isiraeli kuposa mafumu onse a Isiraeli amene anakhalapo iye asanakhale mfumu. 34  Mʼmasiku ake, Hiyeli wa ku Beteli anamanga Yeriko. Atangoyala maziko ake, Abiramu mwana wake woyamba anafa, ndipo atangoika zitseko zake zapageti, Segubu mwana wake womaliza anafa. Izi zinachitika mogwirizana ndi mawu a Yehova amene analankhula kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.+

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “aliyense wokodzera khoma.” Amenewa ndi mawu onyoza a Chiheberi otanthauza mwamuna.
Kapena kuti, “kaya amene akanatha kubwezera magazi ake.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mbuye.”
Kutanthauza, “La Banja la Semeri.”
Talente imodzi inali yofanana ndi makilogalamu 34.2. Onani Zakumapeto B14.