1 Mafumu 17:1-24

  • Mneneri Eliya analosera chilala (1)

  • Akhwangwala ankabweretsera Eliya chakudya (2-7)

  • Eliya anapita kwa mkazi wamasiye wa ku Zarefati (8-16)

  • Mwana wa mkazi wamasiye anamwalira nʼkuukitsidwa (17-24)

17  Eliya*+ wa ku Tisibe, wochokera ku Giliyadi anauza Ahabu+ kuti: “Ndikulumbira mʼdzina la Yehova Mulungu wamoyo, Mulungu wa Isiraeli amene ndimamʼtumikira, sikubwera mame kapena mvula zaka zikubwerazi, pokhapokha ine nditanena.”+  Kenako Eliya anamva mawu a Yehova akuti:  “Uchoke kuno nʼkulowera chakumʼmawa ndipo ukabisale mʼchigwa* cha Keriti chimene chili kumʼmawa kwa Yorodano.  Uzikamwa madzi mumtsinje umene uli mʼchigwacho ndipo ndidzalamula akhwangwala kuti azikakupatsa chakudya.”+  Nthawi yomweyo, Eliya anachita zimene Yehova ananena. Anapita kukakhala mʼmbali mwa chigwa cha Keriti, chakumʼmawa kwa Yorodano.  Akhwangwala ankamubweretsera mkate ndi nyama mʼmawa ndi madzulo, ndipo iye ankamwa madzi mumtsinje umene unali mʼchigwacho.+  Koma patapita masiku angapo,+ mtsinjewo unauma chifukwa mʼdzikomo simunkagwa mvula.  Kenako anamva mawu a Yehova akuti:  “Nyamuka, upite ku Zarefati mʼdziko la Sidoni ukakhale kumeneko. Ine ndikalamula mayi wamasiye kuti azikakupatsa chakudya.”+ 10  Choncho Eliya ananyamuka nʼkupita ku Zarefati. Atafika pageti la mzindawo anaona mayi wamasiye akutola nkhuni. Ndiyeno anamuitana nʼkumuuza kuti: “Mundipatseko madzi pangʼono mʼkapu kuti ndimwe.”+ 11  Atanyamuka kuti akatenge madziwo, anamuitananso nʼkumuuza kuti: “Mundibweretserekonso kamkate pangʼono.” 12  Atamva zimenezi mayiyo anati: “Ndikulumbira mʼdzina la Yehova Mulungu wanu wamoyo, ndilibe mkate, koma ufa pangʼono mumtsuko waukulu ndi mafuta pangʼono mumtsuko waungʼono.+ Panopa ndikutola tinkhuni kuti ndipite kukaphika chakudya choti ineyo ndi mwana wanga tidye. Tikadya, tiziyembekezera kufa.” 13  Ndiyeno Eliya anamuuza kuti: “Musaope. Pitani mukachite zimene mwanenazo. Koma pa zimene muli nazozo, mukayambe mwakonza kaye kamkate kozungulira nʼkundibweretsera. Kenako mukakonze chakudya chanu ndi mwana wanu. 14  Chifukwa Yehova Mulungu wa Isiraeli wanena kuti, ‘Ufa umene uli mumtsuko waukulu suutha ndipo mafuta amene ali mumtsuko waungʼono saatha, mpaka tsiku limene Yehova adzagwetse mvula.’”+ 15  Choncho mayiyo anapita nʼkukachita zimene Eliya ananena. Ndipo iye, banja lake komanso Eliyayo anadya kwa masiku ambiri.+ 16  Ufa umene unali mumtsuko waukulu sunathe, ndipo mafuta amene anali mumtsuko waungʼono sanathe, mogwirizana ndi zimene Yehova ananena kudzera mwa Eliya. 17  Kenako mwana wamwamuna wa mayiyo anadwala. Matenda ake anakula kwambiri mpaka anamwalira.+ 18  Zitatero, mayiyo anauza Eliya kuti: “Ndakulakwirani chiyani inu munthu wa Mulungu woona? Kodi mwabwera kudzandikumbutsa zimene ndinalakwitsa komanso kudzapha mwana wanga?”+ 19  Koma Eliya anamuuza kuti: “Bweretsani mwana wanuyo.” Ndiyeno anatenga mwanayo mʼmanja mwa mayi ake nʼkupita naye kuchipinda chapadenga chimene Eliyayo ankakhala, ndipo anamugoneka pabedi lake.+ 20  Kenako anafuulira Yehova kuti: “Inu Yehova Mulungu wanga,+ kodi mukuchitiranso zoipa mayi wamasiye amene ndikukhala nayeyu pomuphera mwana wake?” 21  Ndiyeno anakumbatira mwanayo katatu ali pabedipo nʼkufuulira Yehova kuti: “Inu Yehova Mulungu wanga, chonde chititsani kuti moyo wa mwanayu ubwerere.” 22  Yehova anamva pemphero la Eliya+ ndipo moyo wa mwanayo unabwerera moti anakhalanso wamoyo.+ 23  Eliya anatenga mwanayo nʼkutsika naye kuchokera mʼchipinda chapadenga chija ndipo anapita naye kwa mayi ake. Ndiyeno anati: “Mwana wanu uja tsopano ali moyo.”+ 24  Mayiyo ataona zimenezi anauza Eliya kuti: “Tsopano ndadziwa kuti ndinudi munthu wa Mulungu+ ndipo mawu a Yehova amene mwanena ndi oona.”

Mawu a M'munsi

Kutanthauza “Mulungu wanga ndi Yehova.”