1 Mafumu 2:1-46

  • Davide analangiza Solomo (1-9)

  • Davide anamwalira; Solomo anakhala mfumu (10-12)

  • Zimene Adoniya anachita zinamuphetsa (13-25)

  • Abiyatara anathamangitsidwa; Yowabu anaphedwa (26-35)

  • Simeyi anaphedwa (36-46)

2  Davide atatsala pangʼono kumwalira, anapatsa mwana wake Solomo malangizo awa:  “Ine ndatsala pangʼono kufa, choncho iweyo uchite zinthu mwamphamvu+ ndipo ukhale wolimba mtima.+  Uzimvera Yehova Mulungu wako poyenda mʼnjira zake komanso posunga malamulo ake, ziweruzo zake ndiponso zikumbutso zake mogwirizana ndi mmene anazilembera mʼChilamulo cha Mose.+ Ukatero zinthu zidzakuyendera bwino* pa zonse zimene ungachite ndiponso kulikonse kumene ungapite.  Komanso Yehova adzakwaniritsa zimene analonjeza zokhudza ineyo zakuti: ‘Ana ako akamadzachita zinthu mosamala komanso kuyenda mokhulupirika* pamaso panga ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse,+ anthu a mʼbanja lako adzapitiriza kukhala pampando wachifumu wa Isiraeli.’+  Iweyo ukudziwa bwino zimene Yowabu mwana wa Zeruya anandichitira, anapha akulu awiri a asilikali a Isiraeli, Abineri+ mwana wa Nera ndi Amasa+ mwana wa Yeteri. Iye anakhetsa magazi+ ankhondo pa nthawi yamtendere. Ndipo anadetsa ndi magazi ankhondo lamba amene anali mʼchiuno mwake ndiponso nsapato zimene zinali kuphazi kwake.  Iweyo uchite zinthu mogwirizana ndi nzeru zako ndipo usalole kuti imvi zake zidzapite ku Manda* mwamtendere.+  Koma ana a Barizilai+ wa ku Giliyadi uwasonyeze chikondi chokhulupirika. Akhale mʼgulu la anthu amene azidya patebulo lako, chifukwa anandithandiza+ pa nthawi imene ndinkathawa mchimwene wako Abisalomu.+  Ndiye palinso Simeyi wa ku Bahurimu, mwana wa Gera wa fuko la Benjamini. Iyeyu anandilankhula mawu onyoza kwambiri+ tsiku limene ndinkapita ku Mahanaimu.+ Koma atabwera kudzakumana nane pa Yorodano, ndinamulumbirira pamaso pa Yehova kuti: ‘Sindidzakupha ndi lupanga.’+  Iweyo usangomusiya, umulange,+ poti ndiwe munthu wanzeru ndipo ukudziwa zimene uyenera kumuchita. Uchite zoti imvi zake zipite ku Manda* zili ndi magazi.”+ 10  Kenako Davide anamwalira,* ndipo anaikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide.+ 11  Davide analamulira Isiraeli zaka 40. Ku Heburoni+ analamulira zaka 7, ndipo ku Yerusalemu analamulira zaka 33.+ 12  Ndiyeno Solomo anakhala pampando wachifumu wa Davide bambo ake, ndipo patapita nthawi ufumu wake unakhazikika.+ 13  Kenako Adoniya mwana wa Hagiti anapita kwa Bati-seba, amayi ake a Solomo ndipo iwo anamufunsa kuti: “Kodi nʼkwabwino?” Iye anayankha kuti: “Inde, nʼkwabwino.” 14  Kenako iye anati: “Ndili nanu mawu.” Ndiyeno Bati-seba anati: “Lankhulani.” 15  Adoniya anapitiriza kuti: “Inu mukudziwa kuti ufumu unayenera kukhala wanga, ndipo Aisiraeli onse ankayembekezera kuti ineyo ndikhala mfumu.+ Koma ufumuwo unatembenuka nʼkukhala wa mchimwene wanga, chifukwa Yehova ndi amene anamupatsa ufumuwo.+ 16  Koma ndikufuna kupempha chinthu chimodzi. Chonde musandikanire.” Bati-seba anamuyankha kuti: “Lankhulani.” 17  Kenako Adoniya anati: “Chonde, mukapemphe Mfumu Solomo kuti andipatse Abisagi+ wa ku Sunemu kuti akhale mkazi wanga. Ndikudziwa kuti inuyo sakakukanirani.” 18  Bati-seba atamva zimenezi anati: “Chabwino. Ndikakupempherani kwa mfumu.” 19  Choncho Bati-seba anapita kwa Mfumu Solomo kukafotokoza zomwe Adoniya anamutuma. Atangofika, Solomo anaimirira kuti akumane naye ndipo anamuweramira. Kenako anakhala pampando wake wachifumu nʼkuitanitsa mpando wina ndipo anauika kumanja kwake kuti amayi akewo akhalepo. 20  Ndiyeno Bati-seba anati: “Pali chinthu chachingʼono chimodzi chimene ndikufuna kupempha. Chonde musandikanire.” Mfumuyo inati: “Pemphani amayi, sindikukanirani.” 21  Choncho Bati-seba anapitiriza kuti: “Ndimapempha kuti Abisagi wa ku Sunemu mumupereke kwa mchimwene wanu Adoniya kuti akhale mkazi wake.” 22  Mfumu Solomo inayankha mayi akewo kuti: “Nʼchifukwa chiyani mukupempha kuti Abisagi wa ku Sunemu akhale mkazi wa Adoniya? Ndiyetu mumupempherenso ufumu,+ popeza iye ndi mkulu wanga+ ndipo wansembe Abiyatara ndi Yowabu+ mwana wa Zeruya+ ali kumbali yake.” 23  Kenako Mfumu Solomo analumbira pamaso pa Yehova kuti: “Mulungu andilange mowirikiza ngati Adoniya sanaike moyo wake pangozi popempha zimenezi. 24  Ndikulumbira mʼdzina la Yehova Mulungu wamoyo, amene anandiika pampando wachifumu wa Davide bambo anga komanso amene anachititsa kuti ufumu wanga ukhazikike+ ndiponso kuti pakhale mzere wa banja lachifumu+ mogwirizana ndi zimene analonjeza, lero Adoniya aphedwa.”+ 25  Nthawi yomweyo Mfumu Solomo anatuma Benaya+ mwana wa Yehoyada kuti akaphe Adoniya ndipo anamuphadi. 26  Mfumuyo inauza wansembe Abiyatara+ kuti: “Pita kuminda yako ku Anatoti.+ Umayenera kufa, koma lero sindikupha chifukwa unanyamula Likasa la Yehova Ambuye Wamkulu Koposa pamaso pa Davide bambo anga+ ndiponso chifukwa chakuti unavutika limodzi ndi bambo anga pa nthawi yonse imene ankavutika.”+ 27  Choncho Solomo anachotsa Abiyatara kuti asatumikirenso monga wansembe wa Yehova ndipo izi zinakwaniritsa mawu amene Yehova analankhula ku Silo+ okhudza nyumba ya Eli.+ 28  Yowabu atamva za nkhaniyi, anathawira kuchihema cha Yehova+ nʼkukagwira nyanga za guwa lansembe. Paja Yowabu ankatsatira Adoniya,+ koma sanatsatire Abisalomu.+ 29  Kenako Mfumu Solomo inauzidwa kuti: “Yowabu wathawira kuchihema cha Yehova ndipo ali pambali pa guwa lansembe.” Choncho Solomo anatuma Benaya mwana wa Yehoyada kuti: “Pita ukamuphe!” 30  Benaya anapitadi kuchihema cha Yehova nʼkukamuuza Yowabu kuti: “Mfumu ikuti utuluke.” Koma iye anati: “Ayi! Ndifera momʼmuno.” Ndiyeno Benaya anakauza mfumu kuti: “Yowabu wanena zimenezi, ndipo wandiyankha choncho.” 31  Mfumuyo inamuuza kuti: “Chita zimene wakuuzazo. Ukamuphe nʼkumuika mʼmanda ndipo undichotsere ineyo komanso nyumba ya bambo anga magazi amene Yowabu anakhetsa popanda chifukwa.+ 32  Yehova adzachititsa kuti magazi ake akhale pamutu pake, chifukwa anapha ndi lupanga anthu awiri olungama komanso abwino kuposa iyeyo. Anachita zimenezi Davide bambo anga osadziwa. Iye anapha Abineri+ mwana wa Nera mkulu wa asilikali a Isiraeli+ ndiponso Amasa+ mwana wa Yeteri mkulu wa asilikali a Yuda.+ 33  Magazi awo adzakhala pamutu pa Yowabu ndi pamutu pa mbadwa zake mpaka kalekale.+ Koma mtendere wochokera kwa Yehova ukhale kwa Davide, mbadwa zake, nyumba yake ndiponso mpando wake wachifumu mpaka kalekale.” 34  Kenako Benaya mwana wa Yehoyada anapita kuchihemako nʼkukapha Yowabu ndipo anaikidwa mʼmanda kunyumba kwake mʼchipululu. 35  Zitatero, mfumu inasankha Benaya+ mwana wa Yehoyada kuti akhale mkulu wa asilikali mʼmalo mwa Yowabu, ndipo inasankha wansembe Zadoki+ kuti alowe mʼmalo mwa Abiyatara. 36  Kenako mfumu inaitanitsa Simeyi+ nʼkumuuza kuti: “Umange nyumba yako ku Yerusalemu ndipo uzikhala kumeneko. Usadzachokeko nʼkupita kwina kulikonse. 37  Tsiku limene udzachoke nʼkudutsa chigwa cha Kidironi,+ udziwiretu kuti udzafa. Mlandu wa magazi ako udzakhala pamutu pako.” 38  Simeyi anayankha mfumu kuti: “Mwanena bwino. Ine mtumiki wanu ndichita zimene mbuyanga mfumu mwanena.” Ndipo Simeyi anakhala ku Yerusalemu masiku ambiri. 39  Koma patatha zaka zitatu, akapolo awiri a Simeyi anathawira kwa Akisi+ mwana wa Maaka, mfumu ya ku Gati. Kenako Simeyi anauzidwa kuti: “Akapolo anutu ali ku Gati.” 40  Nthawi yomweyo, Simeyi anakwera bulu wake nʼkupita ku Gati kwa Akisi kukafunafuna akapolo akewo. Simeyi atabwerako ku Gati ndi akapolo akewo, 41  anthu anauza Solomo kuti: “Simeyi anatuluka mu Yerusalemu kupita ku Gati ndipo wabwerako.” 42  Mfumuyo itamva zimenezi inaitanitsa Simeyi nʼkumufunsa kuti: “Kodi sindinakulumbiritse pamaso pa Yehova nʼkukuchenjeza kuti, ‘Tsiku limene udzatuluke nʼkupita kwina kulikonse, udziwiretu kuti udzafaʼ? Ndipo kodi iwe sunandiuze kuti, ‘Mwanena bwino. Ndichita zimene mwanenaziʼ?+ 43  Ndiye nʼchifukwa chiyani sunasunge lumbiro limene unapanga pamaso pa Yehova komanso lamulo limene ndinakupatsa?” 44  Kenako mfumuyo inauza Simeyi kuti: “Iweyo ukudziwa mumtima mwako zoipa zonse zimene unachitira Davide bambo anga.+ Yehova akubwezera pamutu pako zoipa zimene unachita.+ 45  Koma Mfumu Solomo idzadalitsidwa+ ndipo mpando wachifumu wa Davide udzakhazikika pamaso pa Yehova mpaka kalekale.” 46  Ndiyeno mfumuyo inalamula Benaya mwana wa Yehoyada kuti aphe Simeyi ndipo anamuphadi.+ Choncho ufumu unakhazikika mʼmanja mwa Solomo.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “Ukatero udzachita zinthu mwanzeru.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼchoonadi.”
Amenewa ndi manda a anthu onse. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Amenewa ndi manda a anthu onse. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Mʼchilankhulo choyambirira, “anagona limodzi ndi makolo ake.”