1 Mafumu 4:1-34

  • Ulamuliro wa Solomo (1-19)

  • Zinthu zinkayenda bwino mu ulamuliro wa Solomo (20-28)

    • Aliyense anali wotetezeka pansi pa mtengo wake wa mpesa ndi wa mkuyu (25)

  • Nzeru za Solomo ndi miyambi yake (29-34)

4  Mfumu Solomo ankalamulira Isiraeli yense.+  Ndipo anthu amene anali ndi maudindo ndi awa: Azariya mwana wa Zadoki anali wansembe.+  Elihorefi ndi Ahiya ana a Sisa anali alembi,+ ndipo Yehosafati+ mwana wa Ahiludi anali wolemba zochitika.  Benaya+ mwana wa Yehoyada anali mkulu wa asilikali, ndipo Zadoki ndi Abiyatara+ anali ansembe.  Azariya mwana wa Natani+ anali mkulu wa nduna, ndipo Zabudu mwana wa Natani anali wansembe komanso mnzake wa mfumu.+  Ahisara anali woyangʼanira banja lachifumu, ndipo Adoniramu+ mwana wa Abada ankayangʼanira anthu olembedwa ntchito yokakamiza.+  Solomo anali ndi nduna 12 zomwe zinkayangʼanira Aisiraeli onse ndipo zinkabweretsa chakudya kwa mfumu ndi banja lake. Nduna iliyonse inkabweretsa chakudya kwa mwezi umodzi pachaka.+  Mayina a ndunazo anali awa: Mwana wa Hura, ankayangʼanira kudera lamapiri la Efuraimu.  Mwana wa Dekeri, ankayangʼanira ku Makazi, ku Saalibimu,+ ku Beti-semesi ndi ku Eloni-beti-hanani. 10  Mwana wa Hesedi, ankayangʼanira ku Aruboti (dera lake linali Soko ndi dera lonse la Heferi). 11  Mwana wa Abinadabu ankayangʼanira kumapiri onse a Dori (kenako anakwatira Tafati mwana wa Solomo). 12  Baana mwana wa Ahiludi ankayangʼanira ku Taanaki, ku Megido+ ndi ku Beti-seani+ konse, pafupi ndi Zeretani kumunsi kwa Yezereeli, kuchokera ku Beti-seani kukafika ku Abele-mehola mpaka kuchigawo cha Yokimeamu.+ 13  Mwana wa Geberi ankayangʼanira ku Ramoti-giliyadi+ (dera lake linali midzi ingʼonoingʼono ya Yairi+ mwana wa Manase, yomwe ili ku Giliyadi.+ Analinso ndi chigawo cha Arigobi,+ chomwe chili ku Basana.+ Kunali mizinda ikuluikulu 60 yokhala ndi mipanda komanso zotchingira zakopa*). 14  Ahinadabu mwana wa Ido ankayangʼanira ku Mahanaimu.+ 15  Ahimazi ankayangʼanira kudera la Nafitali (anakwatira mwana wina wa Solomo dzina lake Basemati). 16  Baana mwana wa Husai ankayangʼanira kudera la Aseri ndi ku Bealoti. 17  Yehosafati mwana wa Paruwa ankayangʼanira kudera la Isakara. 18  Simeyi+ mwana wa Ela ankayangʼanira kudera la Benjamini.+ 19  Geberi mwana wa Uri ankayangʼanira ku Giliyadi,+ mʼdera la Sihoni+ mfumu ya Aamori ndi la Ogi+ mfumu ya Basana. Panalinso nduna imodzi yomwe inkayangʼanira nduna zonsezi mʼdzikomo. 20  Ayuda ndi Aisiraeli anachuluka kwambiri ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja+ ndipo ankadya, kumwa komanso kusangalala.+ 21  Solomo ankalamulira maufumu onse kuyambira ku Mtsinje*+ mpaka kudziko la Afilisiti nʼkukafika kumalire ndi Iguputo. Maufumuwa ankabweretsa msonkho kwa Solomo komanso kumutumikira kwa moyo wake wonse.+ 22  Chakudya cha tsiku lililonse chakunyumba yachifumu ya Solomo chinkakhala ufa wosalala wokwana miyezo 30 ya kori,* ufa wamba wokwana miyezo 60 ya kori, 23  ngʼombe 10 zodyetsera mʼkhola, ngʼombe 20 zodyetsera kutchire, nkhosa 100, mbawala zamphongo, insa, ngondo ndiponso mbalame zoweta. 24  Iye ankalamulira chilichonse kumbali yakumadzulo kwa Mtsinje,*+ kuchokera ku Tifisa mpaka ku Gaza.+ Ankalamulira mafumu onse a mbali yakumadzulo kwa Mtsinje ndipo mʼzigawo zake zonse munali mtendere.+ 25  Ayuda ndi Aisiraeli ankakhala mwamtendere. Aliyense ankakhala pansi pa mtengo wake wa mpesa ndi mtengo wake wa mkuyu, kuchokera ku Dani mpaka ku Beere-seba, masiku onse a Solomo. 26  Solomo anali ndi makola 4,000* a mahatchi okoka magaleta ake komanso mahatchi* 12,000.+ 27  Nduna zinkapititsa chakudya cha Mfumu Solomo komanso anthu onse amene ankadya ndi mfumuyo. Nduna iliyonse inkapereka chakudya cha mwezi umodzi ndipo inkaonetsetsa kuti ndi chokwanira bwino.+ 28  Ndunazi zinkabweretsanso balere ndi chakudya cha mahatchi okoka magaleta ndiponso cha mahatchi ena. Zinkachipititsa kulikonse komwe chikufunika, aliyense mogwirizana ndi zomwe walamulidwa. 29  Mulungu anapatsa Solomo nzeru, luso lozindikira komanso mtima womvetsa zinthu zambirimbiri ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.+ 30  Nzeru za Solomo zinaposa nzeru za anthu onse a Kumʼmawa komanso nzeru zonse za ku Iguputo.+ 31  Iye anali wanzeru kuposa munthu aliyense. Anali wanzeru kuposa Etani+ mbadwa ya Zera ndiponso Hemani,+ Kalikoli+ ndi Darida ana a Maholi moti anatchuka mʼmitundu yonse yozungulira.+ 32  Anapeka miyambi 3,000+ ndiponso nyimbo zokwana 1,005.+ 33  Ankafotokoza za mitengo, kuyambira mkungudza wa ku Lebanoni mpaka kamtengo ka hisope+ kamene kamamera pakhoma. Ankafotokozanso za zinyama,+ mbalame,+ nyama zokwawa*+ ndiponso nsomba. 34  Anthu ochokera mʼmitundu yonse ankabwera kudzamva nzeru za Solomo, ngakhalenso mafumu onse apadziko lapansi amene anamva za nzeru zake.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “zotchingira zamkuwa.”
Umenewu ndi mtsinje wa Firate.
Muyezo wa kori unali wokwana malita 220. Onani Zakumapeto B14.
Umenewu ndi mtsinje wa Firate.
Nambalayi imapezeka mʼmipukutu ina komanso munkhani zina. Koma mipukutu ina imati 40,000.
Kapena kuti, “komanso amuna okwera pamahatchi.”
Nʼkutheka kuti zikuphatikizaponso tizilombo touluka.