1 Mafumu 8:1-66

  • Anabweretsa Likasa mʼkachisi (1-13)

  • Solomo analankhula ndi anthu (14-21)

  • Pemphero la Solomo lotsegulira kachisi (22-53)

  • Solomo anadalitsa anthu (54-61)

  • Nsembe ndi chikondwerero chotsegulira kachisi (62-66)

8  Pa nthawi imeneyo Solomo anasonkhanitsa+ akulu a Isiraeli, atsogoleri a mafuko ndiponso atsogoleri a nyumba za makolo a Aisiraeli.+ Anabwera kwa Mfumu Solomo ku Yerusalemu kuti akatenge likasa la pangano la Yehova ku Mzinda wa Davide,+ komwe ndi ku Ziyoni.+  Amuna onse a mu Isiraeli anasonkhana kwa Mfumu Solomo pachikondwerero* mʼmwezi wa Etanimu,* womwe ndi mwezi wa 7.+  Choncho Akulu onse a Isiraeli anabwera ndipo ansembe ananyamula Likasa.+  Iwo ananyamula Likasa la Yehova, chihema chokumanako+ komanso zinthu zonse zopatulika zimene zinali mʼchihemacho. Ansembe ndi Alevi anabweretsa zinthuzi.  Mfumu Solomo ndi gulu lonse la Aisiraeli amene anawaitana, anasonkhana patsogolo pa Likasa. Iwo anapereka nsembe+ zosawerengeka za nkhosa ndi ngʼombe.  Kenako ansembe anabweretsa likasa la pangano la Yehova pamalo ake,+ kuchipinda chamkati cha nyumbayo, chomwe ndi Malo Oyera Koposa, ndipo analiika pansi pa mapiko a akerubi.+  Choncho mapiko a akerubiwo anali pamwamba pa Likasa, moti akerubiwo anatchinga pamwamba pa Likasalo ndi mitengo yake yonyamulira.+  Mitengo yonyamulirayo+ inali yaitali moti nsonga zake zinkaonekera ku Malo Oyera kutsogolo kwa chipinda chamkati, koma sizinkaonekera panja. Mitengoyo idakali pomwepo mpaka lero.  Mu Likasalo munalibe chinthu china chilichonse kupatulapo miyala iwiri yosema+ imene Mose anaikamo+ ku Horebe. Anaiikamo pa nthawi imene Yehova anachita pangano+ ndi Aisiraeli, pamene ankachoka mʼdziko la Iguputo.+ 10  Ansembe atatuluka mʼmalo oyera, mtambo+ unadzaza nyumba ya Yehova.+ 11  Chifukwa cha mtambowo, ansembewo analephera kutumikira popeza ulemerero wa Yehova unadzaza nyumba ya Yehovayo.+ 12  Pa nthawiyo Solomo ananena kuti: “Yehova anati adzakhala mumdima wandiweyani.+ 13  Ine ndakwanitsa kukumangirani nyumba yapamwamba yomwe ndi malo okhazikika oti muzikhalamo mpaka kalekale.”+ 14  Kenako mfumu inatembenuka nʼkuyamba kudalitsa gulu lonse la Aisiraeli. Apa nʼkuti Aisiraeli onsewo ataimirira.+ 15  Mfumuyo inati: “Atamandike Yehova Mulungu wa Isiraeli, amene ndi pakamwa pake analonjeza bambo anga Davide ndipo ndi dzanja lake wakwaniritsa zimene ananena zakuti, 16  ‘Kuyambira tsiku limene ndinatulutsa anthu anga Aisiraeli mʼdziko la Iguputo, sindinasankhe mzinda mʼmafuko onse a Isiraeli womangako nyumba ya dzina langa kuti likhale kumeneko.+ Koma ndasankha Davide kuti alamulire anthu anga Aisiraeli.’ 17  Ndipo bambo anga Davide ankafunitsitsa kumanga nyumba ya dzina la Yehova Mulungu wa Isiraeli.+ 18  Koma Yehova anauza Davide bambo anga kuti, ‘Unkafunitsitsa kumanga nyumba ya dzina langa ndipo unachita bwino kulakalaka utachita zimenezi. 19  Koma iweyo sumanga nyumbayi, mʼmalomwake mwana wamwamuna amene udzabereke* ndi amene adzamange nyumba ya dzina langa.’+ 20  Yehova wakwaniritsa zimene analonjeza, chifukwa ndalowa mʼmalo mwa bambo anga Davide ndipo ndakhala pampando wachifumu wa Isiraeli, mogwirizana ndi zimene Yehova analonjeza. Komanso ndamanga nyumba ya dzina la Yehova Mulungu wa Isiraeli.+ 21  Ndiponso mʼnyumbamo ndakonzamo malo oika Likasa, lomwe muli pangano+ limene Yehova anapangana ndi makolo athu pamene ankawachotsa mʼdziko la Iguputo.” 22  Kenako Solomo anaimirira pafupi ndi guwa lansembe la Yehova kutsogolo kwa Aisiraeli onse ndipo anakweza manja ake mʼmwamba.+ 23  Atatero anati: “Inu Yehova Mulungu wa Isiraeli, palibe Mulungu wina wofanana ndi inu+ kumwambako kapena pansi pano. Mumasunga pangano komanso mumasonyeza chikondi chokhulupirika+ kwa anthu amene amakutumikirani ndi mtima wawo wonse.+ 24  Mwakwaniritsa lonjezo limene munalonjeza mtumiki wanu Davide bambo anga. Munalonjeza ndi pakamwa panu ndipo lero mwakwaniritsa ndi dzanja lanu.+ 25  Tsopano inu Yehova Mulungu wa Isiraeli, mukwaniritse lonjezo limene munalonjeza mtumiki wanu Davide bambo anga lakuti, ‘Anthu a mʼbanja lako sadzasiya kukhala pampando wachifumu wa Isiraeli. Chofunika nʼchakuti ana ako asamale mayendedwe awo poyenda mokhulupirika mʼnjira zanga ngati mmene iwe wachitira.’+ 26  Ndiye inu Mulungu wa Isiraeli, zimene munalonjeza mtumiki wanu Davide bambo anga, zikwaniritsidwe chonde. 27  Koma kodi Mulungu angakhaledi padziko lapansi?+ Kumwamba, ngakhalenso kumwamba kwa kumwamba, simungakwaneko.+ Kuli bwanji nyumba imene ndamangayi?+ 28  Inu Yehova Mulungu wanga, mumvetsere pemphero la mtumiki wanu ndi pempho lake lopempha chifundo. Imvani kulira kwanga kopempha thandizo komanso pemphero limene ine mtumiki wanu ndikupemphera kwa inu lero. 29  Maso anu akhale akuyangʼana nyumba ino masana komanso usiku. Akhale akuyangʼana malo amene munanena kuti, ‘Dzina langa lidzakhala kumeneko,’+ kuti mumvetsere pemphero limene mtumiki wanu angapemphere atayangʼana kumalo ano.+ 30  Mumve pemphero lopempha chifundo la mtumiki wanu komanso la anthu anu Aisiraeli, limene angapemphere atayangʼana malo ano. Inuyo mumve muli kumalo anu okhala, kumwamba,+ mumve nʼkukhululuka.+ 31  Munthu akachimwira mnzake, wochimwiridwayo nʼkulumbiritsa* wochimwayo pofuna kutsimikiza kuti sanachimwedi, ndiyeno wochimwayo akabwera patsogolo pa guwa lansembe mʼnyumba muno,+ 32  inu mumve muli kumwamba ndipo muchitepo kanthu posonyeza amene ali wolakwa nʼkumubwezera mogwirizana ndi zochita zake komanso musonyeze amene ali wosalakwa nʼkumupatsa mphoto mogwirizana ndi chilungamo chake.+ 33  Anthu anu Aisiraeli akagonjetsedwa ndi adani awo chifukwa choti ankakuchimwirani,+ ndiyeno abwerera kwa inu nʼkutamanda dzina lanu+ mʼnyumbayi, kupemphera ndiponso kupempha kuti muwachitire chifundo,+ 34  inuyo mumve muli kumwambako ndipo mukhululuke tchimo la anthu anu Aisiraeli nʼkuwabwezeretsa kudziko limene munapatsa iwowo ndiponso makolo awo.+ 35  Kumwamba kukatsekeka, mvula nʼkumakanika kugwa+ chifukwa choti akhala akukuchimwirani,+ ndiyeno iwo nʼkupemphera atayangʼana malo ano, kutamanda dzina lanu ndiponso kusiya machimo awo chifukwa choti mwawapatsa chilango,+ 36  inuyo mumve muli kumwambako ndipo anthu anu Aisiraeli, omwenso ndi atumiki anu, muwakhululukire machimo awo popeza mudzawaphunzitsa+ njira yabwino yoti aziyendamo. Mubweretse mvula mʼdziko lanu+ limene munapatsa anthu anu monga cholowa. 37  Mʼdzikomo mukagwa njala,+ mliri, mphepo yotentha yowononga mbewu, matenda ambewu a chuku,+ dzombe, ziwala zowononga, mliri wamtundu uliwonse, nthenda yamtundu uliwonse komanso adani awo akawaukira mʼmizinda yawo,+ 38  ndiyeno munthu aliyense kapena anthu anu onse Aisiraeli akapereka pemphero lililonse, akapempha kuti muwachitire chifundo+ (chifukwa aliyense akudziwa ululu umene uli mumtima mwake),+ ndiponso akakweza manja awo atayangʼana kunyumbayi, 39  inuyo mumve muli kumwambako, komwe mumakhala+ ndipo mukhululuke+ ndi kuchitapo kanthu. Mupereke mphoto kwa aliyense mogwirizana ndi njira zake zonse,+ chifukwa mukudziwa mtima wake (inu nokha mumadziwa bwino mtima wa munthu aliyense).+ 40  Muchite zimenezi kuti iwo azikuopani masiku onse amene angakhale ndi moyo mʼdziko limene munapatsa makolo athu. 41  Komanso mlendo amene si mmodzi wa anthu anu Aisiraeli, amene wabwera kuchokera kudziko lakutali chifukwa cha dzina lanu*+ 42  (popeza adzamva za dzina lanu lalikulu,+ dzanja lanu lamphamvu ndiponso mkono wanu wokonzeka kuthandiza*), ndipo wabwera nʼkupemphera atayangʼana nyumbayi, 43  inuyo mumve muli kumwambako, kumene mumakhala,+ ndipo muchite zonse zimene mlendoyo wakupemphani. Muchite zimenezi kuti anthu a mitundu yonse yapadziko lapansi adziwe dzina lanu ndiponso akuopeni+ ngati mmene anthu anu Aisiraeli amachitira, komanso adziwe kuti dzina lanu lili panyumba imene ndamangayi. 44  Anthu anu akapita kunkhondo kukamenyana ndi adani awo mmene mwawatumizira,+ ndipo akapemphera+ kwa Yehova atayangʼana kumzinda umene mwasankha+ ndi kunyumba ya dzina lanu imene ndamanga,+ 45  inuyo mumve muli kumwambako pemphero lawo ndi pempho lawo lopempha chifundo, ndipo muonetsetse kuti chilungamo chachitika kwa iwo. 46  Anthu anu akakuchimwirani (popeza palibe munthu amene sachimwa)+ inu nʼkuwakwiyira kwambiri ndiponso kuwapereka kwa adani, adani awowo nʼkuwatenga kupita nawo kudziko lakutali kapena lapafupi,+ 47  ndiyeno iwo nʼkuzindikira kulakwa kwawo mʼdziko limene anawatengeralo+ nʼkulapa,+ ndiponso akapempha chifundo kwa inu mʼdziko la adani awowo+ nʼkunena kuti, ‘Tachimwa, talakwitsa ndiponso tachita zinthu zoipa,’+ 48  nʼkubwerera kwa inu ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse,+ mʼdziko la adani awo amene anawagwira ndiponso akapemphera kwa inu atayangʼana kudziko lawo limene munapatsa makolo awo, mzinda umene mwasankha komanso nyumba ya dzina lanu imene ndamanga,+ 49  inuyo, kumwamba kumene mumakhalako,+ mumve pemphero lawo ndi pempho lawo lopempha chifundo ndipo muonetsetse kuti chilungamo chachitika kwa iwo. 50  Mukhululukire anthu anu amene anakuchimwirani. Muwakhululukire zimene anakulakwirani. Muchititse kuti adani awo amene anawatenga azikhudzidwa mtima ndipo aziwamvera chisoni,+ 51  (popeza amenewa ndi anthu anu ndi cholowa chanu,+ amene munawatulutsa mu Iguputo,+ kuwachotsa mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo).+ 52  Makutu anu amve pempho* la mtumiki wanu lopempha chifundo+ komanso pempho la anthu anu Aisiraeli lopempha chifundo, powamvera zonse zimene angakupempheni.+ 53  Chifukwa munawasankha pakati pa mitundu yonse ya anthu apadziko lapansi+ kuti akhale cholowa chanu ngati mmene munanenera kudzera mwa Mose mtumiki wanu, pamene munkatulutsa makolo athu mu Iguputo, inu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa.” 54  Solomo atamaliza kupemphera kwa Yehova pemphero lonseli ndiponso kupempha chifundo, anachoka patsogolo pa guwa lansembe la Yehova, chifukwa nthawi yonseyi anali atagwada nʼkukweza manja ake mʼmwamba.+ 55  Kenako anaimirira nʼkuyamba kudalitsa gulu lonse la Aisiraeli ndi mawu okweza kuti: 56  “Atamandike Yehova amene wapatsa anthu ake Aisiraeli malo oti azikhalamo mwamtendere, mogwirizana ndi zimene analonjeza.+ Palibe mawu amene sanakwaniritsidwe pa malonjezo ake onse abwino amene iye analonjeza kudzera mwa Mose mtumiki wake.+ 57  Yehova Mulungu wathu akhale nafe ngati mmene anakhalira ndi makolo athu.+ Asatisiye kapena kutitaya.+ 58  Atipatse mtima wofuna kuyenda mʼnjira zake zonse+ komanso kutsatira malamulo ake, malangizo ake ndi ziweruzo zake zimene analamula makolo athu. 59  Mawu amene ndanenawa popempha chifundo kwa Yehova, Yehova Mulungu wathu aziwakumbukira masana komanso usiku, kuti aonetsetse kuti chilungamo chachitika kwa mtumiki wake ndiponso kwa anthu ake Aisiraeli, mogwirizana ndi zimene zingafunike tsiku lililonse. 60  Achite zimenezi kuti anthu a mitundu yonse yapadziko lapansi adziwe kuti Yehova ndi Mulungu woona+ ndipo palibenso wina.+ 61  Choncho muzitumikira Yehova Mulungu wathu ndi mtima wathunthu+ potsatira malangizo ake ndi kusunga malamulo ake ngati mmene mukuchitira lero.” 62  Kenako mfumu ndi Aisiraeli onsewo anayamba kupereka nsembe zambiri kwa Yehova.+ 63  Solomo anapereka nsembe zamgwirizano+ kwa Yehova. Anapereka ngʼombe 22,000 ndi nkhosa 120,000. Choncho mfumuyo ndi Aisiraeli onse anatsegulira nyumba ya Yehova.+ 64  Tsiku limenelo, mfumu inapatula pakati pa bwalo la nyumba ya Yehova chifukwa inkafunika kuperekerapo nsembe zopsereza, nsembe zambewu komanso mafuta a nsembe zamgwirizano. Inachita zimenezi chifukwa guwa lansembe lakopa*+ lapatsogolo pa kachisi wa Yehova linali lalingʼono kwambiri moti nsembe zopsereza, nsembe zambewu ndiponso mafuta+ a nsembe zamgwirizano sizikanakwanapo. 65  Pa nthawiyo Solomo anachita chikondwerero+ pamodzi ndi Aisiraeli onse. Linali gulu lalikulu la anthu amene anachokera ku Lebo-hamati* nʼkutsetsereka mpaka kukafika kuchigwa* cha Iguputo.+ Anachita chikondwererochi pamaso pa Yehova Mulungu wathu masiku 7, ndi masiku enanso 7. Onse pamodzi masiku 14. 66  Tsiku lotsatira,* Solomo anauza anthuwo kuti azipita, ndipo anthuwo anadalitsa mfumuyo nʼkumapita kwawo. Anapita akusangalala, ali ndi chimwemwe mumtima chifukwa cha zabwino zonse+ zimene Yehova anachitira Davide mtumiki wake komanso anthu ake Aisiraeli.

Mawu a M'munsi

Chimenechi ndi Chikondwerero cha Misasa.
Mʼchilankhulo choyambirira, “wotuluka mʼchiuno mwako.”
Kapena kuti, “nʼkutemberera.” Limeneli ndi lumbiro limene linkachititsa kuti munthu atembereredwe ngati walumbira monama kapena ngati sanakwaniritse zomwe walumbirazo.
Kapena kuti, “mbiri yanu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mkono wanu wotambasula.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Maso anu aone pempho.”
Kapena kuti, “lamkuwa.”
Kapena kuti, “polowera ku Hamati.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “la 8.” Limeneli linali tsiku la 8, atatha masiku 7 achiwiri aja.