1 Mbiri 14:1-17

  • Ufumu wa Davide unakhazikika (1, 2)

  • Banja la Davide (3-7)

  • Afilisiti anagonjetsedwa (8-17)

14  Hiramu+ mfumu ya Turo anatumiza anthu oti akapereke uthenga kwa Davide. Anatumizanso matabwa a mkungudza, anthu oswa miyala ndi kumanga makoma ndiponso akalipentala kuti akamangire Davide nyumba.*+  Davide anadziwa kuti Yehova wachititsa kuti ufumu wake ukhazikike mu Isiraeli,+ popeza ufumu wakewo unakwezedwa kwambiri chifukwa cha anthu a Mulungu, Aisiraeli.+  Ku Yerusalemu, Davide anakwatiranso akazi ena+ ndipo anaberekanso ana ena aamuna ndi aakazi.+  Ana amene Davide anabereka ku Yerusalemu mayina awo+ ndi awa: Samuwa, Sobabu, Natani,+ Solomo,+  Ibara, Elisua, Elipeleti,  Noga, Nefegi, Yafiya,  Elisama, Beliyada ndi Elifeleti.  Afilisiti atamva kuti Davide amudzoza kukhala mfumu ya Aisiraeli onse,+ Afilisiti onse anabwera kudzafunafuna Davide.+ Davide atamva zimenezi, anapita kukamenyana nawo.  Kenako Afilisitiwo anayamba kuukira anthu okhala mʼchigwa cha Arefai.+ 10  Ndiyeno Davide anafunsira kwa Mulungu kuti: “Kodi ndipite kukamenyana ndi Afilisitiwa? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anauza Davide kuti: “Pita, amenewa ndiwaperekadi mʼmanja mwako.”+ 11  Choncho Davide anapita ku Baala-perazimu+ ndipo anapha Afilisiti kumeneko. Ndiyeno Davide anati: “Mulungu woona wawononga adani anga ngati madzi achigumula pogwiritsa ntchito dzanja langa.” Nʼchifukwa chake malowo anawapatsa dzina lakuti Baala-perazimu.* 12  Afilisiti anasiya milungu yawo kumeneko ndipo Davide atalamula, milunguyo anaitentha pamoto.+ 13  Patapita nthawi, Afilisiti aja anabweranso nʼkuyamba kuukira anthu okhala mʼchigwacho.+ 14  Ndiyeno Davide anafunsiranso kwa Mulungu ndipo Mulungu woonayo anamuyankha kuti: “Usapite kukakumana nawo. Uwazembere kumbuyo nʼkuwaukira kutsogolo kwa zitsamba za baka.*+ 15  Ndiyeno ukakamva phokoso la kuguba pamwamba pa zitsamba za bakazo, ukatuluke nʼkuyamba kumenyana nawo chifukwa Mulungu woona adzakhala atatsogola kukapha asilikali a Afilisiti.”+ 16  Choncho Davide anachitadi zimene Mulungu woona anamulamula,+ moti iwo anapha asilikali a Afilisiti kuchokera ku Gibiyoni mpaka ku Gezeri.+ 17  Davide anatchuka mpaka mbiri yake inamveka kumayiko onse ndipo Yehova anachititsa kuti anthu a mitundu yonse azimuopa Davideyo.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “nyumba yachifumu.”
Kutanthauza, “Ambuye wa Zigumula.”
Dzina lakuti “baka” ndi lochokera ku Chiheberi. Chitsamba chimenechi sichikudziwika kuti chinali chotani.