1 Mbiri 22:1-19
22 Kenako Davide anati: “Malo ano ndi nyumba ya Yehova Mulungu woona ndipo lili apali, ndi guwa lansembe zopsereza za Isiraeli.”+
2 Atatero, Davide analamula kuti asonkhanitse alendo okhala mʼdziko la Isiraeli.+ Alendowo anawapatsa ntchito yosema miyala, kuti azisema miyala yomangira nyumba ya Mulungu woona.+
3 Komanso Davide anasonkhanitsa zitsulo zambirimbiri zopangira misomali ya zitseko za mageti ndiponso zopangira zida zopanira zinthu. Anasonkhanitsanso kopa* wambirimbiri wosatheka kumuyeza kulemera kwake.+
4 Davide anasonkhanitsanso matabwa osawerengeka a mkungudza,+ popeza Asidoni+ ndi anthu a ku Turo+ anali atamubweretsera matabwa ambirimbiri a mkungudza.
5 Kenako Davide anati: “Mwana wanga Solomo ndi wamngʼono komanso sadziwa zambiri+ ndipo nyumba yoti adzamangire Yehova idzakhala yaikulu, yokongola+ ndi yogometsa+ nʼcholinga choti idzakhale yodziwika padziko lonse.+ Ndiye ndimukonzera zipangizo zoti adzagwiritsire ntchito.” Choncho Davide asanafe, anasonkhanitsa zipangizo zambirimbiri pokonzekera ntchitoyo.
6 Komanso anaitana mwana wake Solomo ndipo anamupatsa malangizo okhudza ntchito yomanga nyumba ya Yehova Mulungu wa Isiraeli.
7 Davide anauza mwana wake Solomo kuti: “Ineyo ndinkafunitsitsa kumanga nyumba ya dzina la Yehova Mulungu wanga.+
8 Koma Yehova anandiuza kuti: ‘Iweyo wapha anthu* ambirimbiri ndipo wamenya nkhondo zikuluzikulu. Sudzamanga nyumba ya dzina langa,+ chifukwa wapha anthu ambirimbiri pamaso panga padziko lapansi.
9 Tamvera, udzabereka mwana.+ Mwana ameneyo adzakhala munthu wokonda mtendere ndipo ndidzachititsa kuti azikhala mwamtendere komanso asamavutitsidwe ndi adani ake omuzungulira.+ Nʼchifukwa chake dzina lake adzakhala Solomo*+ ndipo mʼmasiku ake ndidzapatsa Aisiraeli bata ndi mtendere.+
10 Iyeyo ndi amene adzamange nyumba ya dzina langa.+ Adzakhala mwana wanga ndipo ine ndidzakhala bambo ake.+ Ndidzakhazikitsa mpando wake wachifumu mu Isiraeli ndipo udzakhalapo mpaka kalekale.’+
11 Tsopano mwana wanga, Yehova akhale nawe ndipo zinthu zikuyendere bwino. Umange nyumba ya Yehova Mulungu wako, mogwirizana ndi zimene iye analankhula zokhudza iweyo.+
12 Yehova akupatse nzeru ndi kuzindikira.+ Akupatsenso mphamvu zotsogolera Aisiraeli, kuti usunge chilamulo cha Yehova Mulungu wako.+
13 Zinthu zidzakuyendera bwino ukamatsatira mosamala malamulo+ ndi ziweruzo zimene Yehova analamula Mose kuti apatse Aisiraeli.+ Khala wolimba mtima ndipo uchite zinthu mwamphamvu. Usaope kapena kuchita mantha.+
14 Ndayesetsa mwakhama kusonkhanitsa golide womangira nyumba ya Yehova wokwana matalente* 100,000 ndi siliva wokwana matalente 1 miliyoni. Koma nʼzosatheka kuyeza kulemera kwa kopa ndi zitsulo+ chifukwa nʼzochuluka kwambiri. Ndasonkhanitsanso matabwa ndi miyala+ pokonzekera, koma udzawonjezerapo zina.
15 Palinso antchito ambirimbiri. Pali osema miyala, amisiri a miyala+ ndi a matabwa ndiponso akatswiri a ntchito zosiyanasiyana.+
16 Golide, siliva, kopa ndi zitsulo nʼzosatheka kuziwerenga.+ Yamba kugwira ntchito imeneyi ndipo Yehova akhale nawe.”+
17 Kenako Davide analamula akalonga onse a Isiraeli kuti athandize mwana wake Solomo. Iye anati:
18 “Kodi Yehova Mulungu wanu sali nanu? Kodi sanakupatseni mtendere mʼdziko lonseli? Chifukwa wandipatsa anthu amʼdzikoli ndipo dzikoli lili mʼmanja mwa Yehova ndi anthu ake.
19 Choncho muzifunafuna Yehova Mulungu wanu+ ndi mtima wanu wonse ndiponso moyo wanu wonse. Yambani kumanga nyumba yopatulika ya Yehova Mulungu woona,+ kuti mukatenge likasa la pangano la Yehova ndi ziwiya zopatulika za Mulungu woona+ nʼkuziika mʼnyumba ya dzina la Yehova imene imangidweyo.”+
Mawu a M'munsi
^ Kapena kuti, “mkuwa.”
^ Kapena kuti, “wakhetsa magazi.”
^ Kuchokera ku mawu a Chiheberi otanthauza, “Mtendere.”
^ Talente imodzi inali yofanana ndi makilogalamu 34.2. Onani Zakumapeto B14.