1 Samueli 24:1-22

  • Davide sanaphe Sauli (1-22)

    • Davide analemekeza wodzozedwa wa Yehova (6)

24  Sauli atangobwerera kuchokera kothamangitsa Afilisiti, anauzidwa kuti: “Davide ali mʼchipululu cha Eni-gedi.”+  Ndiyeno Sauli anatenga amuna 3,000 osankhidwa mu Isiraeli monse, ndipo anapita mʼmatanthwe amene munkakhala mbuzi zamʼmapiri kukafunafuna Davide ndi amuna amene ankayenda naye.  Kenako, Sauli anafika kumakola a nkhosa amiyala mʼmbali mwa msewu, kumene kunali phanga. Iye analowa mʼphangamo kukadzithandiza. Pa nthawiyi nʼkuti Davide ndi amuna amene ankayenda naye atakhala pansi kumbuyo kwa phangalo pamalo osaonekera.+  Amuna amene anali ndi Davidewo anamuuza kuti: “Lerotu ndi tsiku limene Yehova akukuuzani kuti, ‘Taona, ndapereka mdani wako mʼmanja mwako,+ ndipo ukhoza kumuchita chilichonse chimene ukufuna.’” Choncho Davide ananyamuka ndipo mwakachetechete anadula kansalu kamʼmunsi mwa mkanjo wodula manja wa Sauli.  Koma kenako Davide anayamba kuvutika mumtima*+ chifukwa anadula kansalu kamʼmunsi mwa mkanjo wodula manja wa Sauli.  Iye anauza anthu amene anali naye kuti: “Ndikaiona nkhaniyi mmene Yehova akuionera, ndikuona kuti sindingayerekeze kuchitira zimenezo mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Sindingamuchitire zoipa chifukwa iye ndi wodzozedwa wa Yehova.”+  Choncho ndi mawu amenewa, Davide analetsa* anthu amene anali naye kuti asachitire Sauli choipa chilichonse. Kenako Sauli anatuluka mʼphangamo nʼkumapita.  Nayenso Davide anatuluka mʼphangamo ndipo anaitana Sauli kuti: “Mbuyanga mfumu!”+ Sauli atatembenuka, Davide anagwada nʼkuwerama mpaka nkhope yake kufika pansi.  Ndiyeno Davide anauza Sauli kuti: “Nʼchifukwa chiyani mukumvera zimene anthu akunena zakuti, ‘Davide akufuna kukuchitirani zoipa?’+ 10  Lero mwaona nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphangamu. Winawake anandiuza kuti ndikupheni,+ koma ndinakumverani chisoni nʼkunena kuti, ‘Sindingachitire zoipa mbuyanga, chifukwa ndi wodzozedwa wa Yehova.’+ 11  Bambo anga, onani kansalu aka, kamʼmunsi mwa mkanjo wanu wodula manja. Pamene ndimadula kansalu kameneka sindinakupheni. Ndiye mukhoza kuona kuti ndilibe maganizo oipa kapena oukira, ndipo sindinakuchimwireni.+ Koma inuyo mukufunafuna moyo wanga kuti mundiphe.+ 12  Yehova aweruze pakati pa ine ndi inu,+ ndipo Yehova abwezere mʼmalo mwa ine,+ koma dzanja langali silidzakuchitirani choipa.+ 13  Paja mwambi wakale umati, ‘Choipa chimachokera kwa munthu woipa,’ koma dzanja langa silidzakuchitirani choipa. 14  Kodi mfumu ya Isiraeli ikusakasaka ndani? Kodi mukuthamangitsa ndani? Zoona mukuthamangitsa galu wakufa? Nthata imodzi?+ 15  Yehova akhale woweruza, ndipo aweruze pakati pa ine ndi inu. Iye adzaona nkhaniyi nʼkundiweruza kuti ndine wosalakwa+ ndipo adzandipulumutsa mʼmanja mwanu.” 16  Davide atangomaliza kulankhula mawu amenewa, Sauli anati: “Kodi ndi mawu ako, mwana wanga Davide?”+ Kenako Sauli anayamba kulira mokweza. 17  Iye anauza Davide kuti: “Ndiwe wolungama kwambiri kuposa ine, chifukwa wandichitira zabwino, koma ine ndakubwezera zoipa.+ 18  Lero wandiuza zabwino zimene wandichitira, chifukwa sunandiphe pamene Yehova anandipereka mʼmanja mwako.+ 19  Ndi ndani amene angapeze mdani wake nʼkumusiya kuti apite mwamtendere? Yehova adzakupatsa zinthu zabwino+ chifukwa cha zimene wandichitira lero. 20  Ine ndikudziwa kuti iweyo udzakhala mfumu,+ ndipo ufumu wa Isiraeli udzakhalabe mʼmanja mwako. 21  Tsopano ndilumbirire mʼdzina la Yehova+ kuti sudzawononga mbadwa* zanga komanso sudzafafaniza dzina langa mʼnyumba ya bambo anga.”+ 22  Kenako, Davide analumbirira Sauli ndipo Sauliyo anapita kwawo.+ Koma Davide ndi amuna amene anali naye anapita kumalo ovuta kufikako.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “kuvutika chikumbumtima.”
Mabaibulo ena amati, “anabalalitsa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mbewu.”