Kalata Yachiwiri Yopita kwa Akorinto 3:1-18
3 Kodi tikuyambanso kudzichitira umboni tokha? Kapena kodi nʼkofunika kuti ifenso, mofanana ndi anthu ena, tikhale ndi makalata otichitira umboni obwera kwa inu kapena ochokera kwa inu?
2 Inuyo ndinu kalata yathu,+ yolembedwa mʼmitima yathu, yodziwika ndiponso yowerengedwa ndi anthu onse.
3 Chifukwa zikuonekeratu kuti ndinu kalata yochokera kwa Khristu yolembedwa ndi ifeyo atumiki a Mulungu.+ Kalatayo si yolembedwa ndi inki koma ndi mzimu wa Mulungu wamoyo. Si yolembedwa pazolembapo zamiyala+ koma mʼmitima.*+
4 Kudzera mwa Khristu, tikhoza kunena zimenezi molimba mtima pamaso pa Mulungu.
5 Sitinganene kuti ndife oyenera kugwira ntchito imeneyi chifukwa cha mphamvu zathu, koma ndife oyenera kugwira ntchitoyi chifukwa cha Mulungu,+
6 ndipo iyeyo anationa kuti ndife oyenera kukhala atumiki a pangano latsopano,+ osati kudzera mʼmalamulo olembedwa,+ koma kudzera mu mzimu. Malamulo olembedwa amaweruza munthu kuti afe,+ koma mzimu umapatsa munthu moyo.+
7 Malamulo amene amachititsa kuti munthu afe, amenenso analembedwa pamiyala,+ anabwera ndi ulemerero waukulu kwambiri moti Aisiraeli sanathe kuyangʼanitsitsa nkhope ya Mose chifukwa inkawala ndi ulemerero+ umene unatha patapita nthawi.
8 Ndiye kodi mzimu sukuyenera kuperekedwa+ ndi ulemerero waukulu kuposa pamenepa?+
9 Ngati malamulo oweruza anthu kuti alangidwe+ anaperekedwa ndi ulemerero,+ chilungamo chikuyenera kuperekedwa ndi ulemerero woposa pamenepo.+
10 Nawonso malamulo olembedwa amene anapatsidwa ulemerero, achotsedwa ulemererowo chifukwa ulemerero umene wabwera pambuyo pake ndi waukulu kuposa woyambawo.+
11 Ngati malamulo olembedwa, amene anatha patapita nthawi, anaperekedwa ndi ulemerero,+ ndiye kuti malamulo amene sadzatha adzakhala ndi ulemerero waukulu kuposa pamenepo.+
12 Popeza tili ndi chiyembekezo chimenechi,+ tili ndi ufulu wambiri wolankhula,
13 osati ngati Mose amene ankaphimba nkhope yake ndi nsalu,+ kuti Aisiraeli asaone kutha kwa ulemerero wosakhalitsawo.
14 Ndipo maganizo awo anachita khungu.+ Mpaka lero, nsaluyo imakhalabe yophimba pangano lakale likamawerengedwa,+ chifukwa imachotsedwa kudzera mwa Khristu basi.+
15 Ndipotu mpaka pano, zimene Mose analemba zikamawerengedwa,+ mitima yawo imakhalabe yophimba.+
16 Koma munthu akasintha nʼkuyamba kulambira Yehova,* chophimbacho chimachotsedwa.+
17 Yehova* ndi Mzimu+ ndipo pamene pali mzimu wa Yehova,* pali ufulu.+
18 Tonsefe tili ndi nkhope zosaphimba ndipo tili ngati magalasi amene amaonetsa ulemerero wa Yehova.* Tikamaonetsa ulemererowu, timasintha nʼkukhala ngati chifaniziro chake ndipo timaonetsa ulemerero wowonjezerekawonjezereka* mofanana ndendende ndi mmene Yehova,* amene ndi Mzimu, watisinthira.+
Mawu a M'munsi
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “zolembapo zamnofu, mʼmitima.”
^ Onani Zakumapeto A5.
^ Onani Zakumapeto A5.
^ Onani Zakumapeto A5.
^ Onani Zakumapeto A5.
^ Mabaibulo ena amati, “mwa mzimu wa Yehova.”
^ Onani Zakumapeto A5.