2 Mbiri 3:1-17

  • Solomo anayamba kumanga kachisi (1-7)

  • Malo Oyera Koposa (8-14)

  • Zipilala ziwiri zakopa (15-17)

3  Kenako Solomo anayamba kumanga nyumba ya Yehova+ ku Yerusalemu paphiri la Moriya,+ pamalo amene Yehova anaonekera kwa Davide+ bambo ake. Anamanga nyumbayo pamalo amene Davide anali atakonza, pamalo opunthira mbewu a Orinani+ Muyebusi.  Iye anayamba kumanga nyumbayi pa tsiku lachiwiri mʼmwezi wachiwiri, mʼchaka cha 4 cha ufumu wake.  Maziko amene Solomo anayala omangira nyumba ya Mulungu woona, mogwirizana ndi muyezo wakale, anali mikono* 60 mulitali ndi mikono 20 mulifupi.+  Khonde lakutsogolo linali mikono 20 mulitali ndipo linkafanana ndi mulifupi mwa nyumbayo. Kuchoka pansi kufika pamwamba, khondelo linali lalitali 120* ndipo mkati mwake anakutamo ndi golide woyenga bwino.+  Nyumba yaikuluyo anaikuta ndi matabwa a mitengo ya junipa,* kenako anaikutanso ndi golide wabwino.+ Atatero, anaikongoletsa ndi matcheni+ ndiponso zithunzi za mitengo yakanjedza zojambula mochita kugoba.+  Anakongoletsanso nyumbayo poikuta ndi miyala yamtengo wapatali.+ Golide+ wakeyo anali wochokera ku Paravaimu.  Ndipo matabwa ake akudenga, pamakomo, makoma ndi zitseko za nyumbayo anazikuta ndi golide.+ Pamakoma ake anajambulapo akerubi mochita kugoba.+  Kenako iye anapanga chipinda cha Malo Oyera Koposa.+ Mulitali mwake chinali mikono 20 mofanana ndi mulifupi mwa nyumbayo ndipo mulifupi mwake chinali mikono 20. Anachikuta ndi golide wabwino wokwana matalente* 600.+  Golide wa misomali yake anali wolemera masekeli* 50 ndipo zipinda zake zapadenga anazikuta ndi golide. 10  Mʼchipinda cha Malo Oyera Koposa anapangamo zifaniziro ziwiri za akerubi nʼkuzikuta ndi golide.+ 11  Mapiko a akerubiwo+ anali aatali mikono 20. Phiko limodzi la kerubi woyamba linali lalitali mikono 5 ndipo linagunda khoma la chipindacho. Phiko lina linalinso lalitali mikono 5 ndipo linakagunda phiko la kerubi wina. 12  Phiko limodzi la kerubi winayo linali lalitali mikono 5 ndipo linagunda khoma lina la chipindacho. Phiko lina linalinso lalitali mikono 5 ndipo linakagunda phiko la kerubi woyamba uja. 13  Mapiko otambasula a akerubiwo anali aatali mikono 20. Akerubiwo anali ataimirira ndipo nkhope zawo zinayangʼana mkati.* 14  Iye anapanganso katani*+ pogwiritsa ntchito ulusi wabuluu, ubweya wapepo, nsalu yofiira ndi nsalu yabwino kwambiri. Kenako anajambulapo akerubi.+ 15  Kutsogolo kwa nyumbayo anamangako zipilala ziwiri+ zazitali mikono 35. Mutu wa chipilala chilichonse unali wautali mikono 5.+ 16  Atatero anapanganso matcheni okhala ngati ovala mʼkhosi nʼkuwaika pamwamba pa zipilalazo ndipo anapanga makangaza* 100 nʼkuwaika kumatcheniwo. 17  Zipilalazo anaziika kutsogolo kwa kachisi, china anachiika kumanja* china kumanzere.* Chipilala chakumanja anachipatsa dzina lakuti Yakini* ndipo chakumanzere anachipatsa dzina lakuti Boazi.*

Mawu a M'munsi

Mkono umodzi ndi wofanana ndi masentimita 44 ndi hafu. Koma ena amaona kuti mawu akuti “muyezo wakale” amatanthauza mkono wautali womwe unali masentimita 51.8. Onani Zakumapeto B14.
Sizikudziwika kuti 120 inali mikono kapena chiyani.
Mitengo ya junipa ndi yofanana ndi mitengo ya mkungudza.
Talente imodzi inali yofanana ndi makilogalamu 34.2. Onani Zakumapeto B14.
Sekeli imodzi inali yofanana ndi magalamu 11.4. Onani Zakumapeto B14.
Kapena kuti, “zinayangʼana mʼMalo Oyera.”
Kapena kuti, “nsalu yotchinga.”
“Makangaza” ndi mtundu wa chipatso. Ena amati chimanga chachizungu.
Kapena kuti, “kumʼmwera.”
Kapena kuti, “kumpoto.”
Kutanthauza “Iye [Yehova] Akhazikitse.”
Nʼkutheka kuti likutanthauza “Mu Mphamvu.”